Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 71:10 - Buku Lopatulika

Pakuti adani anga alankhula za ine; ndipo iwo akulalira moyo wanga apangana upo,

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Pakuti adani anga alankhula za ine; ndipo iwo akulalira moyo wanga apangana upo,

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Adani anga amandinena, anthu olondalonda moyo wanga amapangana limodzi,

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Pakuti adani anga ayankhula motsutsana nane; iwo amene amadikira kuti andiphe amapangana pamodzi.

Onani mutuwo



Masalimo 71:10
13 Mawu Ofanana  

Alalira monga mkango m'ngaka mwake; alalira kugwira wozunzika, agwira wozunzika, pakumkola mu ukonde mwake.


Ichi chikhale mphotho ya otsutsana nane yowapatsa Yehova, ndi ya iwo akunenera choipa moyo wanga.


Adzikhazikitsa mafumu a dziko lapansi, nachita upo akulu pamodzi, Kutsutsana naye Yehova, ndi Wodzozedwa wake, ndi kuti,


Pakuti ndamva ugogodi wa ambiri, mantha andizinga. Pondipangira chiwembu, anatsimikiza mtima kulanda moyo wanga.


Amemezana, alalira, atchereza mapazi anga, popeza alindira moyo wanga.


Apangana mochenjerera pa anthu anu, nakhalira upo pa obisika anu.


Akanena, Idza nafe, tibisalire mwazi, tilalire osachimwa opanda chifukwa;


Pakuti ndamva kugogodera kwa ambiri, mantha pozungulira ponse. Neneza, ndipo tidzamneneza iye, ati atsamwali anga onse, amene ayang'anira kutsimphina kwanga; kapena adzakopedwa, ndipo ife tidzampambana iye, ndipo tidzambwezera chilango.


Ndipo pakudza mamawa, ansembe aakulu ndi akulu a anthu onse anakhala upo wakumchitira Yesu, kuti amuphe;


Ndipo Saulo anatumiza mithenga kunyumba ya Davide imdikire, ndi kumupha m'mawa; koma Mikala mkazi wa Davide anamuuza, nati, Ukapanda kupulumutsa moyo wako usiku uno, udzaphedwa ndithu m'mawa.