Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 7:13 - Buku Lopatulika

Ndipo anamkonzera zida za imfa; mivi yake aipanga ikhale yansakali.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo anamkonzera zida za imfa; mivi yake aipanga ikhale yansakali.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Wakonza zida zake zoopsa, waika mivi yamoto ku uta wake.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mulungu wakonza zida zake zoopsa; Iye wakonzekera mivi yake yoyaka moto.

Onani mutuwo



Masalimo 7:13
17 Mawu Ofanana  

Pakuti mivi ya Wamphamvuyonse yandilowa, mzimu wanga uwumwa ulembe wake; zoopsa za Mulungu zindindandira nkhondo.


Pakuti, onani, oipa akoka uta, apiringidza muvi wao pansinga, kuwaponyera mumdima oongoka mtima.


Ng'animitsani mphezi, ndi kuwabalalitsa; tumizani mivi yanu, ndi kuwapirikitsa.


Ndipo anatuma mivi yake nawabalalitsa; inde mphezi zaunyinji, nawamwaza.


Mivi yanu njakuthwa; mitundu ya anthu igwa pansi pa inu; iwalasa mumtima adani a mfumu.


Amene anola lilime lao ngati lupanga, napiringidza mivi yao, ndiyo mau akuwawitsa;


Koma Mulungu adzawaponyera muvi; adzalaswa modzidzimutsa.


Wathifula uta wake ngati mdani, waima ndi dzanja lake lamanja ngati mmaliwongo; wapha onse okondweretsa maso; watsanulira ukali wake ngati moto pahema wa mwana wamkazi wa Ziyoni.


Dzuwa ndi mwezi zinaima njera mokhala mwao; pa kuunika kwa mivi yanu popita iyo. Pa kung'anipa kwa nthungo yanu yonyezimira.


Munatulukira chipulumutso cha anthu anu, chipulumutso cha odzozedwa anu; munakantha mutu wa nyumba ya woipa, ndi kufukula maziko kufikira m'khosi.


Ndidzawaunjikira zoipa; ndidzawathera mivi yanga.


ndikanola lupanga langa lonyezimira, ndi dzanja langa likagwira chiweruzo; ndidzabwezera chilango ondiukira, ndi kulanga ondida.


Mivi yanga ndiiledzeretsa nao mwazi, ndi lupanga langa lidzalusira nyama; ndi mwazi wa ophedwa ndi ogwidwa, ndi mutu wachitsitsi wa mdani.


popeza nkolungama kwa Mulungu kubwezera chisautso kwa iwo akuchitira inu chisautso,


popeza anatsanulira mwazi wa oyera mtima, ndi wa aneneri, ndipo mudawapatsa mwazi amwe; ayenera iwo.


ndipo anafuula ndi mau aakulu, ndi kunena, Kufikira liti, Mfumu yoyera ndi yoona, muleka kuweruza ndi kubwezera chilango chifukwa cha mwazi wathu, pa iwo akukhala padziko?