Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 7:10 - Buku Lopatulika

Chikopa changa chili ndi Mulungu, wopulumutsa oongoka mtima.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Chikopa changa chili ndi Mulungu, wopulumutsa oongoka mtima.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Mulungu ndiye chishango changa, amapulumutsa anthu olungama mtima.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chishango changa ndi Mulungu Wammwambamwamba, amene amapulumutsa olungama mtima.

Onani mutuwo



Masalimo 7:10
15 Mawu Ofanana  

Zitapita izo, mau a Yehova anadza kwa Abramu m'masomphenya, kuti, Usaope, Abramu, Ine ndine chikopa chako ndi mphotho yako yaikulukulu.


Ndipo iwe Solomoni mwana wanga, umdziwe Mulungu wa atate wako, umtumikire ndi mtima wangwiro ndi moyo waufulu; pakuti Yehova asanthula mitima yonse, nazindikira zolingirira zonse za maganizo; ukamfunafuna Iye udzampeza, koma ukamsiya Iye adzakusiya kosatha.


pamenepo mumvere mu Mwamba mokhala Inumo, nimukhululukire, ndi kubwezera aliyense monga mwa njira zake zonse, monga mudziwa mtima wake; pakuti Inu, Inu nokha, mudziwa mitima ya ana a anthu;


ukakhala woyera ndi woongoka mtima, zoonadi adzakugalamukira tsopano, ndi kupindulitsa pokhala pako polungama.


Mbeu yake idzakhala yamphamvu padziko lapansi; mbadwo wa oongoka mtima udzadalitsidwa.


Chitirani chokoma, Yehova, iwo okhala okoma; iwo okhala oongoka mumtima mwao.


Ndipo Inu Yehova, ndinu chikopa changa; ulemerero wanga, ndi wondiweramutsa mutu wanga.


Pakuti Yehova Mulungu ndiye dzuwa ndi chikopa; Yehova adzapatsa chifundo ndi ulemerero; sadzakaniza chokoma iwo akuyenda angwiro.


Pakuti chikopa chathu chifuma kwa Yehova; ndi mfumu yathu kwa Woyera wa Israele.


Okhota mtima anyansa Yehova; koma angwiro m'njira zao amsekeretsa.


Pakuti oongoka mtima adzakhala m'dziko, angwiro nadzatsalamo.


Woyenda mwangwiro adzapulumuka; koma wokhota m'mayendedwe ake adzagwa posachedwa.


Koma, Yehova wa makamu, amene aweruza molungama, amene ayesa impso ndi mtima, ndikuoneni Inu mulikuwabwezera chilango, pakuti kwa Inu ndawulula mlandu wanga.


Ine Yehova ndisanthula mtima, ndiyesa impso, kuti ndimpatse munthu yense monga mwa njira zake, monga zipatso za ntchito zake.