Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 75 - Buku Lopatulika


Mulungu woweruza asiyanitsa pakati pa odzikuza ndi olungama
Kwa Mkulu wa Nyimbo: Altasyeti. Salimo la Asafu. Nyimbo.

1 Tikuyamikani Inu, Mulungu; tiyamika, pakuti dzina lanu lili pafupi; afotokozera zodabwitsa zanu.

2 Pakuona nyengo yake ndidzaweruza molunjika.

3 Lasungunuka dziko lapansi, ndi onse okhalamo; ndinachirika mizati yake.

4 Ndinati kwa odzitamandira, musamachita zodzitamandira; ndi kwa oipa, Musamakweza nyanga;

5 musamakwezetsa nyanga yanu; musamalankhula ndi khosi louma.

6 Pakuti kukuzaku sikuchokera kum'mawa, kapena kumadzulo, kapena kuchipululu.

7 Pakuti Mulungu ndiye woweruza; achepsa wina, nakuza wina.

8 Pakuti m'dzanja la Yehova muli chikho; ndi vinyo wake achita thovu; chidzala ndi zosakanizira, ndipo atsanulako. Indedi, oipa onse a padziko lapansi adzamwa nadzagugudiza nsenga zake.

9 Koma ine ndidzalalikira kosalekeza, ndidzaimbira zomlemekeza Mulungu wa Yakobo.

10 Ndipo ndidzatseteka nyanga zonse za oipa; koma nyanga za wolungama zidzakwezeka.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa