Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 75:2 - Buku Lopatulika

2 Pakuona nyengo yake ndidzaweruza molunjika.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

2 Pakuona nyengo yake ndidzaweruza molunjika.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

2 Inu mukuti, “Pa nthaŵi imene ndiisankhule, ndidzaweruza mwachilungamo.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mumati, “Ine ndimayika nthawi yoyenera, ndine amene ndimaweruza mwachilungamo.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 75:2
12 Mawu Ofanana  

Ndipo anthu Ayuda anabwera namdzoza Davide pomwepo akhale mfumu ya nyumba ya Yuda. Ndipo wina anauza Davide kuti, Anthu a ku Yabesi-Giliyadi ndiwo amene anamuika Saulo.


Chomwecho akulu onse a Israele anadza kwa mfumu ku Hebroni; ndipo mfumu Davide anapangana nao pangano ku Hebroni pamaso pa Yehova; ndipo anamdzoza Davide mfumu ya Israele.


Ndipo Davide anakhala mfumu ya Aisraele onse, Davide naweruza ndi chilungamo milandu ya anthu onse.


Ndidzachita mwanzeru m'njira yangwiro; mudzandidzera liti? Ndidzayenda m'nyumba mwanu ndi mtima wangwiro.


Inu mudzauka, ndi kuchitira nsoni Ziyoni; popeza yafika nyengo yakumchitira chifundo, nyengo yoikika.


Ndinati mumtima wanga, Mulungu adzaweruza wolungama ndi woipa; pakuti pamenepo pali mphindi ya zofuna zonse ndi ntchito zonse.


Yehova, Inu ndinu Mulungu wanga, ndidzakukuzani Inu, ndidzatamanda dzina lanu, chifukwa mwachita zinthu zodabwitsa, ngakhale zauphungu zakale, mokhulupirika ndi m'zoonadi.


Chifukwa chake Yesu ananena nao, Nthawi yanga siinafike; koma nthawi yanu yakonzeka masiku onse.


Koma anati kwa iwo, Sikuli kwa inu kudziwa nthawi kapena nyengo, zimene Atate anaziika mu ulamuliro wake wa Iye yekha.


chifukwa anapangira tsiku limene adzaweruza dziko lokhalamo anthu m'chilungamo, ndi munthu amene anamuikiratu; napatsa anthu onse chitsimikizo, pamene anamuukitsa Iye kwa akufa.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa