Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 85:2 - Buku Lopatulika

Munachotsa mphulupulu ya anthu anu, munafotsera zolakwa zao zonse.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Munachotsa mphulupulu ya anthu anu, munafotsera zolakwa zao zonse.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Mudakhululukira machimo a anthu anu, mudafafaniza zolakwa zao zonse.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Munakhululukira mphulupulu za anthu anu ndi kuphimba machimo awo onse. Sela

Onani mutuwo



Masalimo 85:2
10 Mawu Ofanana  

Atero Kirusi mfumu ya ku Persiya, Yehova Mulungu Wam'mwamba anandipatsa maufumu onse a padziko lapansi, nandilangiza ndimmangire nyumba mu Yerusalemu, ndiwo mu Yuda.


Pobweza Yehova ukapolo wa Ziyoni, tinakhala ngati anthu akulota.


Wodala munthuyo wokhululukidwa tchimo lake; wokwiriridwa choipa chake.


Koma Iye pokhala ngwa chifundo, anakhululukira choipa, osawaononga; nabweza mkwiyo wake kawirikawiri, sanautse ukali wake wonse.


Masiku omwewo, nthawi yomweyo, ati Yehova, zoipa za Israele zidzafunidwa, koma zidzasoweka; ndi zochimwa za Yuda, koma sizidzapezeka; pakuti ndidzakhululukira iwo amene ndidzawasiya ngati chotsala.


Ndani Mulungu wofanana ndi Inu, wakukhululukira mphulupulu, wakupitirira zolakwa za otsala a cholowa chake? Sasunga mkwiyo wake kunthawi yonse popeza akondwera nacho chifundo.


Khululukiranitu mphulupulu ya anthu awa, monga mwa chifundo chanu chachikulu, ndi monga mudalekerera anthu awa, kuyambira Ejipito kufikira tsopano.


ndipo mwa Iye yense wokhulupirira ayesedwa wolungama kumchotsera zonse zimene simunangathe kudzichotsera poyesedwa wolungama ndi chilamulo cha Mose.


Ndipo inu, pokhala akufa m'zolakwa ndi kusadulidwa kwa thupi lanu, anakupatsani moyo pamodzi ndi Iye, m'mene adatikhululukira ife zolakwa zonse;