Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 85 - Buku Lopatulika


Akumbutsa Mulungu madalitso akale, apempha awabwereze
Kwa Mkulu wa Nyimbo: Salimo la ana a Kora.

1 Munachita zovomereza dziko lanu, Yehova; munabweza ukapolo wa Yakobo.

2 Munachotsa mphulupulu ya anthu anu, munafotsera zolakwa zao zonse.

3 Munabweza kuzaza kwanu konse; munabwerera kumkwiyo wanu wotentha.

4 Mutibweze, Mulungu wa chipulumutso chathu, nimuletse udani wanu wa pa ife.

5 Kodi mudzatikwiyira nthawi zonse? Kodi mudzakhala chikwiyire mibadwomibadwo?

6 Kodi simudzatipatsanso moyo, kuti anthu anu akondwerere ndi Inu?

7 Tionetseni chifundo chanu, Yehova, tipatseni chipulumutso chanu.

8 Ndidzamva cholankhula Mulungu Yehova; pakuti adzalankhula zamtendere ndi anthu ake, ndi okondedwa ake; koma asabwererenso kuchita zopusa.

9 Indedi chipulumutso chake chili pafupi ndi iwo akumuopa Iye; kuti m'dziko mwathu mukhale ulemu.

10 Chifundo ndi choonadi zakomanizana; chilungamo ndi mtendere zapsompsonana.

11 Choonadi chiphukira m'dziko; ndi chilungamo chasuzumira chili m'mwamba.

12 Inde Yehova adzapereka zokoma; ndipo dziko lathu lidzapereka zipatso zake.

13 Chilungamo chidzamtsogolera; ndipo chidzamkonzera mapazi ake njira.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa