Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 7:3 - Buku Lopatulika

Yehova Mulungu wanga, ngati ndachita ichi; ngati m'manja anga muli chosalungama;

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Yehova Mulungu wanga, ngati ndachita ichi; ngati m'manja anga muli chosalungama;

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Chauta Mulungu wanga, ngati ndachita izi: kumchimwira munthu aliyense,

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Inu Yehova Mulungu wanga, ngati ndachita izi ndipo ndapezeka wolakwa,

Onani mutuwo



Masalimo 7:3
14 Mawu Ofanana  

Mukakhala mphulupulu m'dzanja lako, uichotseretu kutali, ndi chisalungamo chisakhale m'mahema mwako.


Ng'ombe zamphongo zambiri zandizinga; mphongo zolimba za ku Basani zandizungulira.


Landitsani moyo wanga kulupanga; wokondedwa wanga kumphamvu ya galu,


Pakuti onani, alalira moyo wanga; amphamvu andipangira chiwembu, osachimwa, osalakwa ine, Yehova,


Ndikadasekera zopanda pake m'mtima mwanga, Ambuye sakadamvera.


Yehova Chauta Mulungu, Yehova Chauta Mulungu, Iye adziwa, ndi Israele adzadziwa; ngati mopikisana, ngati molakwira Yehova,


Chifukwa chake uchitire kapolo wako zokoma mtima; popeza wamchititsa kapolo wako kupangana nawe pangano la kwa Yehova; koma ngati mwa ine muli choipa chilichonse, undiphe wekha; udzapita nane bwanji kwa atate wako?


Ndipo Saulo anati kwa iye, Munapangana chiwembu pa ine bwanji, iwe ndi mwana wa Yese, kuti unampatsa iye mkate, ndi lupanga, ndi kumfunsira kwa Mulungu kuti iye andiukire, kundilalira, monga lero lomwe?


kuti inu nonse munapangana chiwembu pa ine, ndipo palibe wina wakundiululira kuti mwana wanga anapangana pangano ndi mwana wa Yese, ndipo palibe wina wa inu wakundichitira chifundo kapena kundidziwitsa kuti mwana wanga anafulumiza mnyamata wanga kundilalira monga lero lomwe?


Ndiponso atate wanga, penyani, inde penyani mkawo wa mwinjiro wanu m'dzanja langa; popeza ndinadula mkawo wa mwinjiro wanu, osakuphani, mudziwe, nimuone kuti mulibe choipa kapena kulakwa m'dzanja langa, ndipo sindinakuchimwirani, chinkana inu musaka moyo wanga kuti muugwire.


Davide nanena ndi Saulo, Bwanji mulikusamalira mau a anthu akuti, Onani, Davide afuna kukuchitirani choipa.