Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Masalimo 7:3 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

3 Inu Yehova Mulungu wanga, ngati ndachita izi ndipo ndapezeka wolakwa,

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

3 Yehova Mulungu wanga, ngati ndachita ichi; ngati m'manja anga muli chosalungama;

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

3 Yehova Mulungu wanga, ngati ndachita ichi; ngati m'manja anga muli chosalungama;

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

3 Chauta Mulungu wanga, ngati ndachita izi: kumchimwira munthu aliyense,

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 7:3
14 Mawu Ofanana  

ngati utaya tchimo limene lili mʼdzanja lako ndi kusalola choyipa kuti chikhale mʼmoyo mwako,


Ngʼombe zazimuna zandizungulira; ngʼombe zazimuna zamphamvu za ku Basani zandizinga.


Pulumutsani moyo wanga ku lupanga, moyo wanga wopambanawu ku mphamvu ya agalu.


Onani momwe iwo akundibisalira! Anthu owopsa agwirizana zolimbana nane; osati chifukwa cha mlandu kapena tchimo langa, Inu Yehova.


Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga Ambuye sakanamvera;


“Wamphamvu uja, Mulungu ndiye Yehova! Wamphamvu uja Mulungu ndiye Yehova. Iyeyu ndiye akudziwa chifukwa chiyani tinachita zimenezi. Tikufunanso kuti inu mudziwe. Ngati tinachita izi mopandukira ndiponso moonetsa kusakhulupirira Yehova, lero lomwe lino musatisiye ndi moyo.


Koma undikomere mtima ine mtumiki wako, pakuti unapangana nane pangano pamaso pa Yehova. Ngati ndine wolakwa undiphe ndiwe, koma usandipereke kwa abambo ako.”


Sauli anamufunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani iwe ndi mwana wa Yese mwandiwukira ine? Wamupatsa buledi ndi lupanga. Wafunsiranso kwa Yehova zoti andiwukire ndi kundibisalira monga wachita leromu?”


Mwinatu nʼchifukwa chake mwagwirizana zondichita chiwembu. Palibe amene anandiwuza pamene mwana wanga ankapanga pangano ndi mwana wa Yese. Palibe aliyense amene ankalabadirako za ine kapena kundiwuza kuti mwana wanga wautsa mtima wa wantchito wanga kuti andiwukire monga wachitira lero.”


Tsono abambo anga, onanitu kansalu ka mkanjo wanu kali mʼdzanja langali! Popeza kuti ndinatha kudula msonga ya mkanjo wanu koma osakuphani, pamenepo mudziwe kuti ine ndilibe maganizo woti ndikuchiteni choyipa kapena kukuwukirani. Sindinakulakwireni ngakhale kuti inu mukufuna moyo wanga kuti mundiphe.


Anafunsa Sauli kuti, “Nʼchifukwa chiyani mumamvera mawu a anthu kuti, ‘Davide wakukonzerani chiwembu?’


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa