Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 69:1 - Buku Lopatulika

Ndipulumutseni Mulungu; pakuti madzi afikira moyo wanga.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipulumutseni Mulungu; pakuti madzi afikira moyo wanga.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Inu Mulungu, pulumutseni, pakuti madzi ayesa m'khosi.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Pulumutseni Inu Mulungu, pakuti madzi afika mʼkhosi

Onani mutuwo



Masalimo 69:1
15 Mawu Ofanana  

kapena mdima kuti ungaone, ndi madzi aunyinji akumiza.


Zingwe za imfa zinandizinga, ndipo mitsinje ya zopanda pake inandiopsa.


Chifukwa chake oyera mtima onse apemphere kwa Inu, pa nthawi ya kupeza Inu; indetu pakusefuka madzi aakulu sadzamfikira iye.


Madzi akuya aitanizana ndi madzi akuya, pa mkokomo wa matiti anu; mafunde onse a nyondonyondo anandimiza ine.


Mtima wanga usefukira nacho chinthu chokoma. Ndinena zopeka ine za mfumu, lilime langa ndilo peni yofulumiza kulemba.


Mwatitaya Mulungu, mwatipasula; mwakwiya; tibwezereni.


Ndamira m'thope lozama, lopanda poponderapo; ndalowa m'madzi ozama, ndipo chigumula chandimiza.


Mbusa wa Israele, tcherani khutu; inu wakutsogolera Yosefe ngati nkhosa; inu wokhala pa akerubi, walitsani.


Ndipo ndidzayesa chiweruziro chingwe choongolera, ndi chilungamo chingwe cholungamitsira chilili; ndipo matalala adzachotsa pothawirapo mabodza, ndi madzi adzasefukira mobisalamo.


Pamene udulitsa pamadzi ndili pamodzi ndi iwe; ndi pooloka mitsinje sidzakukokolola; pakupyola pamoto sudzapsa; ngakhale lawi silidzakutentha.


madzi anayenda pamwamba pamutu panga, ndinati, Ndalikhidwa.


Ndipo anena ndi ine, Madziwo udawaona uko akhalako mkazi wachigololoyo ndiwo anthu, ndi makamu, ndi mitundu, ndi manenedwe.