Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 60:1 - Buku Lopatulika

1 Mwatitaya Mulungu, mwatipasula; mwakwiya; tibwezereni.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

1 Mwatitaya Mulungu, mwatipasula; mwakwiya; tibwezereni.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

1 Inu Mulungu mwatitaya ife, mwatiwonongera otiteteza. Mwatikwiyira, tibwezeni mwakale.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza. Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 60:1
36 Mawu Ofanana  

Ndipo Hadadezere anatumiza mthenga nakatenga Aaramu a ku tsidya la chimtsinje; iwo nafika ku Helamu, ndi Sobaki kazembe wa khamu la nkhondo la Hadadezere anawatsogolera.


Ndipo Davide anafika ku Baala-Perazimu, nawakantha kumeneko Davideyo; nati, Yehova wathyola adani anga pamaso panga ngati madzi okamulira. Chifukwa chake analitcha dzina la malowo Baala-Perazimu.


Ndipo anaika maboma mu Edomu; m'dziko lonse la Edomu anaika maboma, ndipo Aedomu onse anasanduka anthu a Davide. Ndipo Yehova anasunga Davide kulikonse anamukako.


Davide anakanthanso Hadadezere, mwana wa Rehobu, mfumu ya ku Zoba, pomuka iye kukadzitengeranso ufumu wake ku chimtsinje cha Yufurate.


Anapha Aedomu mu Chigwa cha Mchere zikwi khumi, nalanda Sela ndi nkhondo, nautcha dzina lake Yokotele mpaka lero lino.


Ndipo Davide anakantha Hadadezere mfumu ya Zoba ku Hamati, pomuka iye kukhazikitsa ulamuliro wake ku mtsinje wa Yufurate.


Ndipo iwe Solomoni mwana wanga, umdziwe Mulungu wa atate wako, umtumikire ndi mtima wangwiro ndi moyo waufulu; pakuti Yehova asanthula mitima yonse, nazindikira zolingirira zonse za maganizo; ukamfunafuna Iye udzampeza, koma ukamsiya Iye adzakusiya kosatha.


Nalimbika mtima Amaziya. Natsogolera anthu ake, namuka ku Chigwa cha Mchere, nakantha ana a Seiri zikwi khumi.


Si ndinu Mulungu, amene mwatitaya osatuluka nao magulu athu?


Koma mwatitaya, ndi kutinyazitsa; ndipo simutuluka nao makamu a nkhondo athu.


Ndilanditseni kwa adani anga, Mulungu wanga, ndiikeni pamsanje kwa iwo akundiukira.


Musawapheretu, angaiwale anthu anga, muwabalalitse mwa mphamvu yanu, ndipo muwagwetse, Ambuye, ndinu chikopa chathu.


Si ndinu, Mulungu, amene mwatitaya? Osatuluka nao makamu athu, Mulungu.


Mulungu, munatitayiranji chitayire? Mkwiyo wanu ufukiranji pa nkhosa za kubusa kwanu?


Yehova, mudzakwiya nthawi zonse kufikira liti? Nidzatentha nsanje yanu ngati moto?


Tithandizeni Mulungu wa chipulumutso chathu, chifukwa cha ulemerero wa dzina lanu; ndipo tilanditseni, ndi kutifafanizira zoipa zathu, chifukwa cha dzina lanu.


Mbusa wa Israele, tcherani khutu; inu wakutsogolera Yosefe ngati nkhosa; inu wokhala pa akerubi, walitsani.


Mutibweze, Mulungu; nimuwalitse nkhope yanu, ndipo tidzapulumuka.


Mutibweze, Mulungu wa chipulumutso chathu, nimuletse udani wanu wa pa ife.


Pamenepo munalankhula m'masomphenya ndi okondedwa anu, ndipo mudati, Ndasenza thandizo pa chiphona; ndakweza wina wosankhika mwa anthu.


Ndinachita chipangano ndi wosankhika wanga, ndinalumbirira Davide mtumiki wanga.


Koma Inu munamtaya, nimunamkaniza, munakwiya naye wodzozedwa wanu.


Ndiye Mulungu, ayenera kumuopa kwambiri mu upo wa oyera mtima, ndiye wochititsa mantha koposa onse akumzinga.


Bwerani, Yehova; kufikira liti? Ndipo alekeni atumiki anu.


Ndipo ndidzalimbitsa nyumba ya Yuda, ndi kusunga nyumba ya Yosefe, ndipo ndidzawakhalitsa, pakuti ndawachitira chifundo; ndipo adzakhala monga ngati sindinawataye konse; pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wao, ndipo ndidzawamvera.


Ndipo Samuele anati, Mwachitanji? Nati Saulo, Chifukwa ndinaona kuti anthuwo alinkubalalika kundisiya ine, ndi kuti inu simunafike masiku aja tinapangana, ndi kuti Afilisti anasonkhana ku Mikimasi;


Ndipo wakubwera ndi mauyo anayankha, nati, Israele anathawa pamaso pa Afilisti, ndiponso kunali kuwapha kwakukulu kwa anthu, ndi ana anu awiri omwe Hofeni ndi Finehasi afa, ndipo likasa la Mulungu lalandidwa.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa