Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 49:3 - Buku Lopatulika

Pakamwa panga padzanena zanzeru; ndipo chilingiriro cha mtima wanga chidzakhala cha chidziwitso.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Pakamwa panga padzanena zanzeru; ndipo chilingiriro cha mtima wanga chidzakhala cha chidziwitso.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Zosinkhasinkha za mtima wanga zidzakhala zakuya, ndipo ndidzalankhula zanzeru.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Pakamwa panga padzayankhula mawu anzeru; mawu ochokera mu mtima mwanga adzapereka nzeru.

Onani mutuwo



Masalimo 49:3
15 Mawu Ofanana  

Maneno anga awulula chiongoko cha mtima wanga, ndi monga umo idziwira milomo yanga idzanena zoona.


Ngati mulibe mau, tamverani ine; mukhale chete, ndipo ndidzakuphunzitsani nzeru.


Pomlingirira Iye pandikonde; ndidzakondwera mwa Yehova.


Potsegulira mau anu paunikira; kuzindikiritsa opusa.


Mau a m'kamwa mwanga ndi maganizo a m'mtima wanga avomerezeke pamaso panu, Yehova, thanthwe langa, ndi Mombolo wanga.


Pakamwa pa wolungama palankhula zanzeru, ndi lilime lake linena chiweruzo.


Koma dziwani kuti Yehova anadzipatulira yekha womkondayo, adzamva Yehova m'mene ndimfuulira Iye.


Mtima wanga usefukira nacho chinthu chokoma. Ndinena zopeka ine za mfumu, lilime langa ndilo peni yofulumiza kulemba.


Tchera makutu ako, numvere mau a anzeru, nulozetse mtima wako kukadziwa zanga.


Munthu wabwino atulutsa zabwino m'chuma chake chabwino, ndi munthu woipa atulutsa zoipa m'chuma chake choipa.


Chiphunzitso changa chikhale ngati mvula; maneno anga agwe ngati mame; ngati mvula yowaza pamsipu, ndi monga madontho a mvula pazitsamba.