Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 38:3 - Buku Lopatulika

Mumnofu mwanga mulibe chamoyo chifukwa cha ukali wanu; ndipo m'mafupa anga simuzizira, chifukwa cha cholakwa changa.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Mumnofu mwanga mulibe chamoyo chifukwa cha ukali wanu; ndipo m'mafupa anga simuzizira, chifukwa cha cholakwa changa.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Thupi langa lilibe mphamvu chifukwa cha ukali wanu. M'nkhongono mwanga mwalobodoka chifukwa cha uchimo wanga.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chifukwa cha ukali wanu mulibe thanzi mʼthupi langa; mafupa anga alibe mphamvu chifukwa cha tchimo langa.

Onani mutuwo



Masalimo 38:3
13 Mawu Ofanana  

Koma Uziya anapsa mtima, mbale ya zofukiza ili m'dzanja lake kufukiza nayo; ndipo pakupsa mtima nao ansembe, khate linabuka pamphumi pake, pamaso pa ansembe m'nyumba ya Yehova, pambali pa guwa lofukizapo.


Pakuti mivi ya Wamphamvuyonse yandilowa, mzimu wanga uwumwa ulembe wake; zoopsa za Mulungu zindindandira nkhondo.


Popeza masiku anga akanganuka ngati utsi, ndi mafupa anga anyeka ngati nkhuni.


Chifukwa cha liu la kubuula kwanga mnofu wanga umamatika kumafupa anga.


Chifukwa usana ndi usiku dzanja lanu linandilemera ine; uwisi wanga unasandulika kuuma kwa malimwe.


Mundimvetse chimwemwe ndi kusekera, kuti mafupawo munawathyola akondwere.


Mundichitire chifundo, Yehova; pakuti ndalefuka ine. Mundichize, Yehova; pakuti anthunthumira mafupa anga.