Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 3:6 - Buku Lopatulika

Sindidzaopa unyinji wa anthu akundizinga ine.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Sindidzaopa unyinji wa anthu akundizinga ine.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Sindichita mantha ngakhale adani anga ndi osaŵerengeka, ngakhale andizinge ndi kundithira nkhondo.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Sindidzaopa adani anga osawerengeka amene abwera kulimbana nane kuchokera ku madera onse.

Onani mutuwo



Masalimo 3:6
11 Mawu Ofanana  

Ndipo anthu a Israele anakanthidwa pamenepo pamaso pa anyamata a Davide, ndipo kunali kuwapha kwakukulu kumeneko tsiku lomwelo, anthu zikwi makumi awiri.


Adzikhazikitsa mafumu a dziko lapansi, nachita upo akulu pamodzi, Kutsutsana naye Yehova, ndi Wodzozedwa wake, ndi kuti,


Inde, ndingakhale ndiyenda m'chigwa cha mthunzi wa imfa, sindidzaopa choipa; pakuti Inu muli ndi ine; chibonga chanu ndi ndodo yanu, izi zindisangalatsa ine.


Chifukwa chake sitidzachita mantha, lingakhale lisandulika dziko lapansi, angakhale mapiri asunthika, nakhala m'kati mwa nyanja.


Yehova wa makamu ali ndi ife; Mulungu wa Yakobo ndiye pamsanje pathu.


Ukagona, sudzachita mantha; udzagona tulo tokondweretsa.


Adzakutsogolera ulikuyenda, ndi kukudikira uli m'tulo, ndi kulankhula nawe utauka.


Ndipo tidzatani ndi zinthu izi? Ngati Mulungu ali ndi ife, adzatikaniza ndani?