Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 3 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero


Salimo 3
Salimo la Davide. Atathawa mwana wake Abisalomu.

1 Inu Yehova, achulukadi adani anga! Achulukadi amene andiwukira!

2 Ambiri akunena za ine kuti, “Mulungu sadzamupulumutsa.” Sela

3 Koma Inu Yehova, ndinu chishango chonditeteza, Inu mwandiveka ulemerero ndipo mwanditukula.

4 Kwa Yehova, Ine ndilira mofuwula ndipo Iye amandiyankha kuchokera ku phiri lake loyera. Sela

5 Ine ndimagona ndi kupeza tulo; ndimadzukanso chifukwa Yehova amandichirikiza.

6 Sindidzaopa adani anga osawerengeka amene abwera kulimbana nane kuchokera ku madera onse.

7 Dzukani, Inu Yehova! Pulumutseni, Inu Mulungu wanga. Akantheni adani anga onse pa msagwada; gululani mano a anthu oyipa.

8 Chipulumutso chimachokera kwa Yehova. Madalitso akhale pa anthu anu. Sela

The Word of God in Contemporary Chichewa

Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.®

Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.®

Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.

Biblica, Inc.
Titsatireni:



Zotsatsa