Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 18:1 - Buku Lopatulika

Ndikukondani, Yehova, mphamvu yanga.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndikukondani, Yehova, mphamvu yanga.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ndimakukondani Chauta, Inu mphamvu zanga.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Davide anati: Ine ndimakukondani Inu Yehova, mphamvu zanga.

Onani mutuwo



Masalimo 18:1
18 Mawu Ofanana  

Ndiloleni, Yehova, indetu ndine mtumiki wanu; ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; mwandimasulira zondimanga.


Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; ndipo anakhala chipulumutso changa.


Mulungu ndiye wondizingiza mphamvu m'chuuno, nakonza njira yanga ikhale yangwiro.


Masautso a wolungama mtima achuluka, koma Yehova amlanditsa mwa onsewa.


Cholakwa cha woipayo chimati m'kati mwa mtima wanga, palibe kuopa Mulungu pamaso pake.


Pakutitu, Davide, m'mene adautumikira uphungu wa Mulungu m'mbadwo mwake mwa iye yekha, anagona tulo, naikidwa kwa makolo ake, naona chivundi;


Ndikhoza zonse mwa Iye wondipatsa mphamvuyo.


olimbikitsidwa m'chilimbiko chonse, monga mwa mphamvu ya ulemerero wake, kuchitira chipiriro chonse ndi kuleza mtima konse pamodzi ndi chimwemwe,


Ndipo Mosetu anali wokhulupirika m'nyumba yake yonse, monga mnyamata, achitire umboni izi zidzalankhulidwazi;


Tikonda ife, chifukwa anayamba Iye kutikonda.