Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 16:3 - Buku Lopatulika

Za oyera mtima okhala padziko lapansi, iwo ndiwo omveka mbiri, mwa iwowo muli chikondwero changa chonse.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Za oyera mtima okhala pa dziko lapansi, iwo ndiwo omveka mbiri, mwa iwowo muli chikondwero changa chonse.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Kunena za oyera mtima amene ali pansi pano, ameneŵa ndi olemekezeka, ndipo ndimakondwera nawo.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Kunena za oyera mtima amene ali pa dziko, amenewa ndi olemekezeka, amene ndimakondwera nawo.

Onani mutuwo



Masalimo 16:3
20 Mawu Ofanana  

Ndipo tsopano nyamukani, Yehova Mulungu, kudza kopumulira kwanu, Inu ndi likasa la mphamvu yanu; ansembe anu, Yehova Mulungu, avale chipulumutso; ndi okondedwa anu akondwere nazo zabwino.


Maso anga ayang'ana okhulupirika m'dziko, kuti akhale ndi Ine; iye amene ayenda m'njira yangwiro, iyeyu adzanditumikira Ine.


Imfa ya okondedwa ake nja mtengo wake pamaso pa Yehova.


Ine ndine wakuyanjana nao onse akukuopani, ndi iwo akusamalira malangizo anu.


Chifukwa cha abale anga ndi mabwenzi anga, ndidzanena tsopano, Mukhale mtendere mwa inu.


Imbirani Yehova, inu okondedwa ake, ndipo yamikani pokumbukira chiyero chake.


Wolungama atsogolera mnzake; koma njira ya oipa iwasokeretsa.


Ukayenda ndi anzeru udzakhala wanzeru: koma mnzao wa opusa adzaphwetekedwa.


ndi kukondwera ndi dziko lake lokhalamo anthu, ndi kusekerera ndi ana a anthu.


Ndine wa wokondedwa wanga mnyamatayo, ndine amene andifunayo.


Iwe sudzatchedwanso Wosiyidwa; dziko lako silidzatchedwanso Bwinja; koma iwe udzatchedwa Hefiziba ndi dziko lako Beula; pakuti Yehova akondwera mwa iwe, ndipo dziko lako lidzakwatiwa.


Ndipo adzakhala angaanga, ati Yehova wa makamu, tsiku ndidzaikalo, ndipo ndidzawaleka monga munthu aleka mwana wake womtumikira.


Ndipo Ananiya anayankha nati, Ambuye, ndamva ndi ambiri za munthu uyu, kuti anachitiradi choipa oyera mtima anu mu Yerusalemu;


Chifukwa chake, monga tili nayo nyengo, tichitire onse chokoma, koma makamaka iwo a pa banja la chikhulupiriro.


Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu, mwa chifuniro cha Mulungu, kwa oyera mtima amene ali mu Efeso, ndi kwa iwo okhulupirika mwa Khristu Yesu:


Okhulupirika mauwa, ndipo za izi ndifuna kuti ulimbitse mau, kuti iwo akukhulupirira Mulungu asamalire akhalebe atsogoleri a ntchito zabwino. Izi nzokoma ndi zopindulitsa anthu;


pakuti Mulungu sali wosalungama kuti adzaiwala ntchito yanu, ndi chikondicho mudachionetsera kudzina lake, umo mudatumikira oyera mtima ndi kuwatumikirabe.