Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 146:3 - Buku Lopatulika

Musamakhulupirira zinduna, kapena mwana wa munthu, amene mulibe chipulumutso mwa iye.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Musamakhulupirira zinduna, kapena mwana wa munthu, amene mulibe chipulumutso mwa iye.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Musakhulupirire mafumu kapena anthu ena amene sangathe kuthandiza.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Musamadalire mafumu, anthu osakhalitsa, amene sangathe kupulumutsa.

Onani mutuwo



Masalimo 146:3
11 Mawu Ofanana  

Nati iye, Akapanda kukuthandiza Yehova, ndikaona kuti kokuthandiza ine? Kudwale kodi, kapena popondera mphesa?


Nthawi yomweyi Hanani mlauli anadza kwa Asa mfumu ya Yuda, nanena naye, Popeza mwatama mfumu ya Aramu, osatama Yehova Mulungu wanu, chifukwa chake khamu la nkhondo la mfumu ya Aramu lapulumuka m'dzanja lanu.


Tithandizeni mumsauko; pakuti chipulumutso cha munthu ndi chabe.


Tithandizeni kunsautso; kuti chipulumutso cha munthu ndi chabe.


Indetu, anthu achabe ndi mpweya, ndipo anthu aakulu ndi bodza, pakuwayesa apepuka; onse pamodzi apepuka koposa mpweya.


Siyani munthu, amene mpweya wake uli m'mphuno mwake; chifukwa m'mene awerengedwamo ndi muti?


Tsiku limenelo, ati Yehova wa makamu, chikhomo chokhomeredwa polimba udzasukusika; nudzaguluka, ndi kugwa, ndi katundu wopachikidwapo adzadulidwa; pakuti Yehova wanena.


Koma Aejipito ndiwo anthu, si Mulungu; ndi akavalo ao ali nyama, si mzimu; ndipo pamene Yehova adzatambasula dzanja lake, wothandiza adzaphunthwa, ndi wothandizidwa adzagwa, ndipo iwo onse awiri pamodzi adzalephera.


Ndipo Yesaya anati kwa iwo, Mukati kwa mbuyanu, Atero Yehova, musaope mau amene wawamva iwe, amene atumiki a mfumu ya Asiriya andilalatira Ine.