Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 40:23 - Buku Lopatulika

Nakonzerapo mkate pamaso pa Yehova; monga Yehova adamuuza Mose.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Nakonzerapo mkate pamaso pa Yehova; monga Yehova adamuuza Mose.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

ndipo pamwamba pa tebulolo adaikapo buledi, monga momwe Chauta adamlamulira.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

ndipo anayikapo buledi pamaso pa Yehova, monga momwe Yehova analamulira Mose.

Onani mutuwo



Eksodo 40:23
8 Mawu Ofanana  

Mwa ansembe ake muli Mose ndi Aroni, ndi Samuele mwa iwo akuitanira dzina lake; anaitana kwa Yehova, ndipo Iye anawayankha.


Ndipo uziika mkate woonekera pa gomelo pamaso panga nthawi zonse.


Ndipo anaika choikaponyali m'chihema chokomanako, popenyana ndi gome, pa mbali ya kumwera ya Kachisi.


Ulongenso gomelo, nukonzerepo zokonzera zake; ulongenso choikaponyalicho, ndi kuyatsa nyali zake.


Ndipo uzitenga ufa wosalala, ndi kuphika timitanda khumi ndi tiwiri; awiri a magawo khumi a efa afikane kamtanda kamodzi.


Ndipo utiike m'mizere iwiri, tisanu ndi kamodzi mzere umodzi, pa gome loyera, pamaso pa Yehova.


Kuti analowa m'nyumba ya Mulungu, nadya mikate yoonetsa, imene yosaloleka kudya iye kapena amene anali naye, koma ansembe okhaokha.


Pakuti chihema chidakonzeka, choyamba chija, m'menemo munali choikaponyali, ndi gome, ndi mkate woonekera; paja paitanidwa Malo Opatulika.