Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Samueli 22:5 - Buku Lopatulika

Pakuti mafunde a imfa anandizinga, mitsinje ya zopanda pake inandiopsa ine.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Pakuti mafunde a imfa anandizinga, mitsinje ya zopanda pake inandiopsa ine.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

“Zoŵaŵa za imfa zidandizinga, mitsinje ya ku malo a anthu akufa idandisefukira.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

“Mafunde a imfa anandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.

Onani mutuwo



2 Samueli 22:5
12 Mawu Ofanana  

Zingwe za imfa zinandizinga, ndipo mitsinje ya zopanda pake inandiopsa.


Koma usana Yehova adzalamulira chifundo chake, ndipo usiku nyimbo yake idzakhala ndi ine. Inde pemphero la kwa Mulungu wa moyo wanga.


Chomwecho iwo adzaopa dzina la Yehova kuchokera kumadzulo, ndi ulemerero wake kumene kutulukira dzuwa; pakuti pamene mdani adzafika ngati chigumula, mzimu wa Yehova udzamkwezera mbendera yomletsa.


Pakuti munandiponya mwakuya m'kati mwa nyanja, ndipo madzi anandizinga; mafunde anu onse a nyondonyondo anandimiza.


Koma pamene paliponse mudzaona Yerusalemu atazingidwa ndi magulu a ankhondo, zindikirani pamenepo kuti chipulumutso chake chayandikira.


Pamene angonena, Mtendere ndi mosatekeseka, pamenepo chionongeko chobukapo chidzawagwera, monga zowawa mkazi wa pakati; ndipo sadzapulumuka konse.


Ndipo anadza mmodzi mwa angelo asanu ndi awiri akukhala nazo mbale zisanu ndi ziwiri, nalankhula ndi ine, nanena, Idza kuno, ndidzakuonetsa chitsutso cha mkazi wachigololo wamkulu, wakukhala pamadzi ambiri,


Ndipo anena ndi ine, Madziwo udawaona uko akhalako mkazi wachigololoyo ndiwo anthu, ndi makamu, ndi mitundu, ndi manenedwe.