Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa

Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano


Masalimo 52 - Buku Lopatulika Buku Lopatulika
Masalimo 52

Davide aneneratu za chionongeko cha oipa, iye nakhulupirira Mulungu
Kwa Mkulu wa Nyimbo. Chilangizo cha Davide; muja analowa Doegi Mwedomu nauza Saulo nati kwa iye, Davide walowa m'nyumba ya Ahimeleki.

1 Udzitamandiranji ndi choipa, chiphona iwe? Chifundo cha Mulungu chikhala tsiku lonse.

2 Lilime lako likupanga zoipa; likunga lumo lakuthwa, lakuchita monyenga.

3 Ukonda choipa koposa chokoma; ndi bodza koposa kunena chilungamo,

4 ukonda mau onse akuononga, lilime lachinyengo, iwe.

5 Potero Mulungu adzakupasula kunthawi zonse, adzakuchotsa nadzakukwatula m'hema mwako, nadzakuzula, kukuchotsa m'dziko la amoyo.

6 Ndipo olungama adzachiona, nadzaopa, nadzamseka, ndi kuti,

7 Tapenyani, suyu munthuyu amene sanamuyese Mulungu mphamvu yake; amene anatama kuchuluka kwa chuma chake, nadzilimbitsa m'kuipsa kwake.

8 Koma ine ndine ngati mtengo wauwisi wa azitona m'nyumba ya Mulungu. Ndikhulupirira chifundo cha Mulungu kunthawi za nthawi.

9 Ndidzakuyamikani kosatha, popeza Inu munachichita ichi, ndipo ndidzayembekeza dzina lanu, pakuti ichi nchokoma, pamaso pa okondedwa anu.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi