Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 52:3 - Buku Lopatulika

3 Ukonda choipa koposa chokoma; ndi bodza koposa kunena chilungamo,

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

3 Ukonda choipa koposa chokoma; ndi bodza koposa kunena chilungamo,

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

3 Umakonda zoipa kupambana zabwino, umakonda kunama kupambana kulankhula zoona.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

3 Iwe umakonda choyipa mʼmalo mwa kuyankhula choonadi. Umakonda kunama kupambana kuyankhula zoona. Sela

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 52:3
10 Mawu Ofanana  

Komatu amkhalira upo kuti amkankhire pansi ulemu wake; akondwera nao mabodza; adalitsa ndi m'kamwa mwao, koma atemberera mumtima.


Wamphulupulu mtima wake umkhumba zoipa; sakomera mtima mnzake.


Pakuti anthu anga apusa, sandidziwa Ine; ali ana opulukira sazindikira; ali ochenjera kuchita choipa koma kuchita chabwino sakudziwa.


Lilime lao ndi muvi wakuphera; linena manyengo; wina anena mtendere ndi mnansi wake pakamwa pake, koma m'mtima mwake amlalira.


Inu amene mudana nacho chokoma ndi kukondana nacho choipa; inu akumyula khungu lao pathupi pao, ndi mnofu wao pa mafupa ao;


Inu muli ochokera mwa atate wanu mdierekezi, ndipo zolakalaka zake za atate wanu mufuna kuchita. Iyeyu anali wambanda kuyambira pachiyambi, ndipo sanaime m'choonadi, pakuti mwa iye mulibe choonadi. Pamene alankhula bodza, alankhula za mwini wake; pakuti ali wabodza, ndi atate wake wa bodza.


amenewo anasandutsa choonadi cha Mulungu chabodza napembedza, natumikira cholengedwa, ndi kusiya Wolengayo, ndiye wolemekezeka nthawi yosatha. Amen.


achiwembu, aliuma olimbirira, otukumuka mtima, okonda zokondweretsa munthu, osati okonda Mulungu;


Kunja kuli agalu ndi anyanga, ndi achigololo, ndi ambanda, ndi opembedza mafano, ndi yense wakukonda bodza ndi kulichita.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa