Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 53 - Buku Lopatulika


Kupusa ndi kuipa kwa anthu
( Mas. 14 )
Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Mahalati. Chilangizo cha Davide.

1 Chitsiru chimati mumtima mwake, Kulibe Mulungu. Achita zovunda, achita chosalungama chonyansa; kulibe wakuchita bwino.

2 Mulungu m'mwamba anaweramira pa ana a anthu, kuti aone ngati aliko wanzeru, wakufuna Mulungu.

3 Onse anabwerera; anavunda mtima pamodzi; palibe mmodzi wakuchita bwino, nnena mmodzi.

4 Kodi ochita zopanda pake sadziwa? Pomadya anthu anga monga akudya mkate; ndipo saitana Mulungu.

5 Pamenepo anaopa kwakukulu, popanda chifukwa cha kuopa, pakuti Mulungu anamwaza mafupa a iwo akuzinga iwe; unawachititsa manyazi, pakuti Mulungu anawakaniza.

6 Ha, chipulumutso cha Israele chichokere mu Ziyoni! Pakubweretsa Mulungu anthu ake a m'ndende, Yakobo adzakondwera, Israele adzasekera.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa