Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa

Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano


Masalimo 121 - Buku Lopatulika Buku Lopatulika
Masalimo 121

Mulungu Msungi wokhulupirika wa anthu ake
Nyimbo yokwerera.

1 Ndikweza maso anga kumapiri: Thandizo langa lidzera kuti?

2 Thandizo langa lidzera kwa Yehova, wakulenga kumwamba ndi dziko lapansi.

3 Sadzalola phazi lako literereke: Iye amene akusunga sadzaodzera.

4 Taonani, wakusunga Israele sadzaodzera kapena kugona.

5 Yehova ndiye wakukusunga; Yehova ndiye mthunzi wako wa kudzanja lako lamanja.

6 Dzuwa silidzawamba usana, mwezi sudzakupanda usiku.

7 Yehova adzakusunga kukuchotsera zoipa zilizonse; adzasunga moyo wako.

8 Yehova adzasungira kutuluka kwako ndi kulowa kwako, kuyambira tsopano kufikira nthawi zonse.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi