Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 121:7 - Buku Lopatulika

7 Yehova adzakusunga kukuchotsera zoipa zilizonse; adzasunga moyo wako.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

7 Yehova adzakusunga kukuchotsera zoipa zilizonse; adzasunga moyo wako.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

7 Chauta adzakuteteza ku zoipa zonse, adzasamala moyo wako.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

7 Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse; adzasunga moyo wako.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 121:7
14 Mawu Ofanana  

Taonani, Ine ndili pamodzi ndi iwe, ndipo ndidzakusunga iwe konse kumene upitako, ndipo ndidzakubwezanso iwe ku dziko lino; chifukwa kuti sindidzakusiya iwe, kufikira kuti nditachita chimene ndanena nawe.


Ndipo Yabezi anaitana kwa Mulungu wa Israele, ndi kuti, Mundidalitse ndithu, ndi kukulitsa malire anga; ndi dzanja lanu likhale ndi ine, nimundisunge, kuti choipa chisandivute. Ndipo Mulungu anafikitsa chopempha iye.


Yehova asunga onse akukondana naye; koma oipa onse adzawaononga.


Yehova aombola moyo wa anyamata ake, ndipo sadzawatsutsa kumlandu onse akukhulupirira Iye.


Yehova adzamsunga, nadzamsunga ndi moyo, ndipo adzadalitsika padziko lapansi, ndipo musampereke ku chifuniro cha adani ake.


Inu okonda Yehova, danani nacho choipa: Iye asunga moyo wa okondedwa ake; awalanditsa m'manja mwa oipa.


Palibe vuto lidzagwera wolungama; koma amphulupulu adzadzazidwa ndi zoipa.


Yehova akudalitse iwe, nakusunge;


Ndipo musatitengere kokatiyesa, koma mutipulumutse kwa woipayo.


Ndipo tidziwa kuti amene akonda Mulungu zinthu zonse zithandizana kuwachitira ubwino, ndiwo amene aitanidwa monga mwa kutsimikiza kwa mtima wake.


Ambuye adzandilanditsa ku ntchito yonse yoipa, nadzandipulumutsa ine kulowa Ufumu wake wa Kumwamba; kwa Iye ukhale ulemerero kunthawi za nthawi. Amen.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa