Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 120 - Buku Lopatulika


Apempha Mulungu amlanditse pa omnamiza
Nyimbo yokwerera.

1 Ndinafuulira kwa Yehova mu msauko wanga, ndipo anandivomereza.

2 Yehova, landitsani moyo wanga kumilomo ya mabodza, ndi kulilime lonyenga.

3 Adzakuninkhanji, adzakuonjezeranji, lilime lonyenga iwe?

4 Mivi yakuthwa ya chiphona, ndi makala tsanya.

5 Tsoka ine, kuti ndili mlendo mu Meseki, kuti ndigonera m'mahema a Kedara!

6 Moyo wanga unakhalitsa nthawi pamodzi ndi iye wakudana nao mtendere.

7 Ine ndikuti, Mtendere; koma polankhula ine, iwowa akuti, Nkhondo.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa