Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 120:1 - Buku Lopatulika

1 Ndinafuulira kwa Yehova mu msauko wanga, ndipo anandivomereza.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

1 Ndinafuulira kwa Yehova mu msauko wanga, ndipo anandivomereza.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

1 Ndimalirira Chauta m'mavuto anga kuti andiyankhe.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga, ndipo Iye amandiyankha.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 120:1
31 Mawu Ofanana  

Musandibisire nkhope yanu tsiku la nsautso yanga; munditchereze khutu lanu; tsiku limene ndiitana ine mundiyankhe msanga.


Pamenepo anafuulira kwa Yehova mumsauko mwao, ndipo anawapulumutsa m'kupsinjika kwao.


M'mene ndinasautsika ndinaitanira pa Yehova; anandiyankha nandiika motakasuka Yehova.


Ndikweza maso anga kumapiri: Thandizo langa lidzera kuti?


Ndinakondwera m'mene ananena nane, Tiyeni kunyumba ya Yehova.


Ndikweza maso anga kwa Inu, kwa Inu wakukhala kumwamba.


Akadapanda kukhala nafe Yehova, anene tsono Israele;


Iwo akukhulupirira Yehova akunga phiri la Ziyoni, losasunthika, likhazikika kosatha.


Pobweza Yehova ukapolo wa Ziyoni, tinakhala ngati anthu akulota.


Akapanda kumanga nyumba Yehova, akuimanga agwiritsa ntchito chabe; akapanda kusunga mzinda Yehova, mlonda adikira chabe.


Wodala yense wakuopa Yehova, wakuyenda m'njira zake.


Anandisautsa kawirikawiri kuyambira ubwana wanga, anene tsono Israele;


M'mozamamo ndinakufuulirani, Yehova.


Yehova, mtima wanga sunadzikuze ndi maso anga sanakwezeke; ndipo sindinatsate zazikulu, kapena zodabwitsa zondiposa.


Yehova, kumbukirani Davide kuzunzika kwake konse.


Onani, nkokoma ndi kokondweretsa ndithu kuti abale akhale pamodzi!


Taonani, lemekezani Yehova, atumiki a Yehova inu nonse, akuimirira m'nyumba ya Yehova usiku.


M'kusauka kwanga ndinaitana Yehova, ndipo ndinakuwira Mulungu wanga; mau anga anawamva mu Kachisi mwake, ndipo mkuwo wanga wa pankhope pake unalowa m'makutu mwake.


Ndipo undiitane tsiku la chisautso, ndidzakulanditsa, ndipo iwe udzandilemekeza.


Wopereka nsembe yachiyamiko andilemekeza Ine; ndipo kwa iye wosunga mayendedwe ake ndidzamuonetsa chipulumutso cha Mulungu.


Ndipo anati, Ndinaitana Yehova m'nsautso wanga, ndipo anandiyankha ine; ndinafuula ndili m'mimba ya manda, ndipo munamva mau anga.


Pakuti munandiponya mwakuya m'kati mwa nyanja, ndipo madzi anandizinga; mafunde anu onse a nyondonyondo anandimiza.


Ndipo pokhala Iye m'chipsinjo mtima anapemphera kolimba koposa ndithu: ndi thukuta lake linakhala ngati madontho aakulu a mwazi alinkugwa pansi.


Ameneyo, m'masiku a thupi lake anapereka mapemphero ndi mapembedzero pamodzi ndi kulira kwakukulu ndi misozi kwa Iye amene anakhoza kumpulumutsa Iye muimfa, ndipo anamveka popeza anaopa Mulungu,


Ndipo panali pamene nthawi yake inafika, Hana anaima, nabala mwana wamwamuna; namutcha dzina lake Samuele, nati, Chifukwa ndinampempha kwa Yehova,


Ndinampempha mwanayu; ndipo Yehova anandipatsa chopempha changa ndinachipempha kwa Iye;


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa