Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 96 - Buku Lopatulika


Onse a pansi pano ndi am'mwamba omwe alemekeze Mulungu
( 1Mbi. 16.23-33 )

1 Muimbireni Yehova nyimbo yatsopano; muimbireni Yehova, inu, dziko lonse lapansi.

2 Muimbireni Yehova, lemekezani dzina lake; lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.

3 Fotokozerani ulemerero wake mwa amitundu; zodabwitsa zake mwa mitundu yonse ya anthu.

4 Pakuti Yehova ndi wamkulu, nayenera kulemekezedwa kwakukulu; ayenera amuope koposa milungu yonse.

5 Pakuti milungu yonse ya mitundu ya anthu ndiyo mafano, koma Yehova analenga zakumwamba.

6 Pamaso pake pali ulemu ndi ukulu. M'malo opatulika mwake muli mphamvu ndi zochititsa kaso.

7 Mpatseni Yehova, inu, mafuko a mitundu ya anthu, mpatseni Yehova ulemerero ndi mphamvu.

8 Mpatseni Yehova ulemerero wa dzina lake; bwerani nacho chopereka, ndipo fikani kumabwalo ake.

9 Gwadirani Yehova moyera ndi mokometsetsa, njenjemerani pamaso pake, inu dziko lonse lapansi.

10 Nenani mwa amitundu, Yehova achita ufumu; dziko lokhalamo anthu lomwe likhazikika kuti silingagwedezeke; adzaweruza mitundu ya anthu molunjika.

11 Kumwamba kukondwere nilisekerere dziko lapansi; nyanja ibume mwa kudzala kwake.

12 Munda ukondwerere ndi zonse zili m'mwemo; pamenepo mitengo yonse ya kunkhalango idzafuula mokondwera.

13 Pamaso pa Yehova, pakuti akudza; pakuti akudza kudzaweruza dziko lapansi Adzaweruza dziko lokhalamo anthu ndi chilungamo, ndi mitundu ya anthu ndi choonadi.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa