Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 65 - Buku Lopatulika


Davide alemekeza Mulungu pa madalitso ochuluka
Kwa Mkulu wa Nyimbo: Salimo la Davide. Nyimbo.

1 Mu Ziyoni akulemekezani Inu mwachete, Mulungu, adzakuchitirani Inu chowindachi.

2 Wakumva pemphero Inu, zamoyo zonse zidzadza kwa Inu.

3 Mphulupulu zinandipambana; koma mudzafafaniza zolakwa zathu.

4 Wodala munthuyo mumsankha, ndi kumyandikizitsa, akhale m'mabwalo anu. Tidzakhuta nazo zokoma za m'nyumba yanu, za m'malo oyera a Kachisi wanu.

5 Mudzatiyankha nazo zoopsa m'chilungamo, Mulungu wa chipulumutso chathu; ndinu chikhulupiriko cha malekezero onse a dziko lapansi, ndi cha iwo okhala kutali kunyanja.

6 Ndinu amene mukhazikitsa mapiri ndi mphamvu yanu; pozingidwa nacho chilimbiko.

7 Amene atontholetsa kukuntha kwa nyanja, kukuntha kwa mafunde ake, ndi phokoso la mitundu ya anthu.

8 Ndipo iwo akukhala kumalekezero adzachita mantha chifukwa cha zizindikiro zanu; mukondweretsa apo patulukira dzuwa, ndi apo lilowera.

9 Mucheza nalo dziko lapansi, mulithirira, mulilemeretsa kwambiri; mtsinje wa Mulungu udzala nao madzi, muwameretsera tirigu m'mene munakonzera nthaka.

10 Mukhutitsa nthaka yake yolima; mufafaniza nthumbira zake; muiolowetsa ndi mvumbi; mudalitsa mmera wake.

11 Muveka chakachi ndi ukoma wanu; ndipo mabande anu akukha zakucha.

12 Akukha pa mabusa a m'chipululu; ndipo mapiri azingika nacho chimwemwe.

13 Podyetsa mpodzaza ndi zoweta; ndipo zigwa zakutidwa ndi tirigu; zifuula mokondwera, inde ziimbira.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa