Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 47 - Buku Lopatulika


Mau a kulemekeza Mulungu mwini dziko lonse lapansi
Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la ana a Kora.

1 Ombani m'manja, mitundu yonse ya anthu; fuulirani kwa Mulungu ndi liu la kuimbitsa.

2 Pakuti Yehova Wam'mwambamwamba ndiye woopsa; ndiye mfumu yaikulu padziko lonse lapansi.

3 Atigonjetsera anthu, naika amitundu pansi pa mapazi athu.

4 Atisankhira cholowa chathu, chokometsetsa cha Yakobo amene anamkonda.

5 Mulungu wakwera ndi mfuu, Yehova ndi liu la lipenga.

6 Imbirani Mulungu, imbirani; imbirani mfumu yathu, imbirani.

7 Pakuti Mulungu ndiye mfumu ya dziko lonse lapansi; imbirani ndi chilangizo.

8 Mulungu ndiye mfumu ya amitundu, Mulungu akhala pa mpando wachifumu wake woyera.

9 Akulu a anthu asonkhana akhale anthu a Mulungu wa Abrahamu, pakuti zikopa za dziko lapansi nza Mulungu; akwezeka kwakukulu Iyeyo.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa