Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Yohane 4:3 - Buku Lopatulika

anachokera ku Yudeya, namukanso ku Galileya.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

anachokera ku Yudeya, namukanso ku Galileya.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pamene Yesu adadziŵa kuti Afarisi azimva zimenezi, adachokako ku Yudeya napitanso ku Galileya.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Iye anachoka ku Yudeya ndi kubwereranso ku Galileya.

Onani mutuwo



Yohane 4:3
11 Mawu Ofanana  

Koma pamene angakuzunzeni inu m'mudzi uwu, thawirani mwina: indetu ndinena kwa inu, Simudzaitha mizinda ya Israele, kufikira Mwana wa Munthu atadza.


Ndipo Yesu anachokako pamodzi ndi ophunzira ake nanka kunyanja: ndipo linamtsata khamu lalikulu la a ku Galileya, ndi a ku Yudeya,


Ndipo kunali, pakumuka ku Yerusalemu Iye analikupita pakati pa Samariya ndi Galileya.


M'mawa mwake anafuna kutuluka kunka ku Galileya, napeza Filipo. Ndipo Yesu ananena naye, Tsata Ine.


Ndipo anachoka kunkanso tsidya lija la Yordani, kumalo kumene kunali Yohane analikubatiza poyamba paja; ndipo anakhala komweko.


Chifukwa chake Yesu sanayendeyendenso poonekera mwa Ayuda, koma anachokapo kunka kudziko loyandikira chipululu, kumudzi dzina lake Efuremu; nakhala komweko pamodzi ndi ophunzira ake.


Chiyambi ichi cha zizindikiro zake Yesu anachita mu Kana wa mu Galileya naonetsera ulemerero wake; ndipo ophunzira ake anakhulupirira Iye.


Zitapita izi anadza Yesu ndi ophunzira ake kudziko la Yudeya; ndipo pamenepo anatsotsa nao pamodzi, nabatiza.


Chimene anachiona nachimva, achita umboni wa ichi chomwe; ndipo kulibe munthu alandira umboni wake.


Iyeyu, pamene anamva kuti Yesu wachokera ku Yudeya nafika ku Galileya, ananka kwa Iye, nampempha kuti atsike kukachiritsa mwana wake; pakuti anali pafupi imfa.


Ndipo zitapita izi Yesu anayendayenda mu Galileya; pakuti sanafune kuyendayenda mu Yudeya, chifukwa Ayuda anafuna kumupha Iye.