Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Yohane 1:43 - Buku Lopatulika

43 M'mawa mwake anafuna kutuluka kunka ku Galileya, napeza Filipo. Ndipo Yesu ananena naye, Tsata Ine.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

43 M'mawa mwake anafuna kutuluka kunka ku Galileya, napeza Filipo. Ndipo Yesu ananena naye, Tsata Ine.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

43 M'maŵa mwake Yesu adaganiza zopita ku Galileya. Adapeza Filipo, namuuza kuti, “Unditsate.”

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

43 Pa tsiku lotsatira Yesu anaganiza zopita ku Galileya. Atamupeza Filipo, anati kwa iye, “Nditsate.”

Onani mutuwo Koperani




Yohane 1:43
19 Mawu Ofanana  

Iwo amene sanafunse za Ine andifunafuna; ndi iwo amene sanandipwaire andipeza; ndinati, Taonani Ine, taonani Ine, kwa mtundu umene sunatchule dzina langa.


Filipo, ndi Bartolomeo; Tomasi, ndi Mateyu wamsonkho yo; Yakobo mwana wa Alifeyo, ndi Tadeyo;


Ndipo pamene Yesu anamva kuti anampereka Yohane, anamuka kulowa ku Galileya;


Koma Yesu ananena kwa iye, Tsata Ine, nuleke akufa aike akufa ao.


Ndipo Yesu popita, kuchokera kumeneko, anaona munthu, dzina lake Mateyu, alinkukhala polandirira msonkho, nanena kwa iye, Nditsate Ine. Ndipo iye anauka, namtsata.


Pakuti Mwana wa Munthu anadza kufunafuna ndi kupulumutsa chotayikacho.


Zinthu izi zinachitika mu Betaniya tsidya lija la Yordani, pomwe analikubatiza Yohane.


M'mawa mwake anaona Yesu alinkudza kwa iye, nanena, Onani Mwanawankhosa wa Mulungu amene achotsa tchimo lake la dziko lapansi!


M'mawa mwakenso analikuimirira Yohane ndi awiri a ophunzira ake;


Ndipo ophunzira awiriwo anamva iye alinkulankhula, natsata Yesu.


Koma Filipo anali wa ku Betsaida, mzinda wa Andrea ndi Petro.


Ndipo iwo anadza kwa Filipo wa ku Betsaida wa mu Galileya, namfunsa iye, ndi kuti, Mbuye, tifuna kuona Yesu.


Filipo ananena ndi Iye, Ambuye, tionetsereni ife Atate, ndipo chitikwanira.


Chiyambi ichi cha zizindikiro zake Yesu anachita mu Kana wa mu Galileya naonetsera ulemerero wake; ndipo ophunzira ake anakhulupirira Iye.


Pamenepo Yesu, pokweza maso ake, ndi kuona kuti khamu lalikulu lilinkudza kwa Iye, ananena kwa Filipo, Tidzagula kuti mikate kuti adye awa?


Filipo anayankha Iye, Mikate ya marupiya atheka mazana awiri siikwanira iwo, kuti yense atenge pang'ono.


Si kunena kuti ndinalandira kale, kapena kuti ndatha kukonzeka wamphumphu; koma ndilondetsa, ngatinso ndikachigwire ichi chimene anandigwirira Khristu Yesu.


Tikonda ife, chifukwa anayamba Iye kutikonda.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa