Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Numeri 4:18 - Buku Lopatulika

Musamasadza fuko la mabanja a Akohati kuwachotsa pakati pa Alevi;

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Musamasadza fuko la mabanja a Kohati kuwachotsa pakati pa Alevi;

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

“Musalole kuti a m'banja la Kohati aonongeke pakati pa Alevi.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

“Onetsetsani kuti mabanja a fuko la Kohati asachotsedwe kwa Alevi.

Onani mutuwo



Numeri 4:18
13 Mawu Ofanana  

Ndipo Yehova anati kwa Mose, Tsika, chenjeza anthu, kuti angapyolere kwa Yehova kudzaona, ndipo angagwe ambiri a iwowa.


Aliyense amene akonza ena otere, kapena aliyense awaika pa mlendo, ameneyo asazidwe kwa anthu a mtundu wake.


Aliyense wokonza china chotere kununkhizapo, achotsedwe kwa anthu a mtundu wake.


Ndipo adzatulutsira Ababiloni akazi anu onse, ndi ana anu, ndipo simudzapulumuka m'manja ao, koma mudzagwidwa ndi dzanja la mfumu ya ku Babiloni; ndipo mudzatenthetsa mzindawu ndi moto.


ndi dziko linayasama pakamwa pake ndi kuwameza, iwo ndi mabanja ao, ndi amuna ao onse akutsata Kora, ndi akatundu ao onse.


Ndipo Yehova anati kwa Mose, Bweza ndodo ya Aroni kuiika chakuno cha mboni, isungike ikhale chizindikiro cha pa ana opikisana; kuti unditsirizire madandaulo ao, kuti ungafe.


Ndipo musunge udikiro wa malo opatulika, ndi udikiro wa guwa la nsembe; kuti pasakhalenso mkwiyo pa ana a Israele.


Banja la Aamuramu, ndi banja la Aizihara, ndi banja la Ahebroni, ndi banja la Auziyele ndiwo a Kohati; ndiwo mabanja a Akohati.


Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, nati,


koma muzitero nao kuti akhale ndi moyo, osafa ai, poyandikiza iwo zopatulika kwambirizo; Aroni ndi ana ake aamuna alowe, namuikire munthu yense ntchito yake ndi katundu wake.


Ndipo Mulungu anakantha anthu a ku Betesemesi, chifukwa anasuzumira m'likasa la Yehova, anakantha anthu zikwi makumi asanu; ndipo anthu analira maliro, chifukwa Yehova anawakantha anthuwo ndi makanthidwe aakulu.