Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Numeri 16:32 - Buku Lopatulika

32 ndi dziko linayasama pakamwa pake ndi kuwameza, iwo ndi mabanja ao, ndi amuna ao onse akutsata Kora, ndi akatundu ao onse.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

32 ndi dziko linayasama pakamwa pake ndi kuwameza, iwo ndi mabanja ao, ndi amuna ao onse akutsata Kora, ndi akatundu ao onse.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

32 Nthakayo idayasama ndi kuŵameza onsewo pamodzi ndi mabanja ao ndiponso anthu onse a gulu la Kora ndi zinthu zao zonse.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

32 ndipo dziko linatsekula pakamwa pake ndi kuwameza pamodzi ndi nyumba zawo ndi anthu onse a Kora ndi katundu wawo yense.

Onani mutuwo Koperani




Numeri 16:32
21 Mawu Ofanana  

Tsopano ndiwe wotembereredwa kunthaka, imene inatsegula pakamwa pake kulandira padzanja lako mwazi wa mphwako:


Ana a Kohati: Aminadabu mwana wake, Kora mwana wake, Asiri mwana wake,


mwana wa Tahati, mwana wa Asiri, mwana wa Ebiyasafu, mwana wa Kora,


Dziko lidayasama nilidameza Datani, ndipo linafotsera gulu la Abiramu.


Mafupa athu amwazika pakamwa pa manda, monga ngati akumba nanyimphula nthaka yapansi.


Pokhala Inu mpotikonda ndithu, Yehova wa makamu!


Munachita zovomereza dziko lanu, Yehova; munabweza ukapolo wa Yakobo.


Yehova, Mulungu wa chipulumutso changa, ndinafuula pamaso panu usana ndi usiku.


Dziko lapansi lasweka ndithu, dziko lapansi lasungunukadi, dziko lapansi lili kugwedezeka kopambana.


Ndipo manda akuza chilakolako chake, natsegula kukamwa kwake kosayeseka; ndi ulemerero wao, ndi unyinji wao, ndi phokoso lao, ndi iye amene akondwerera mwa iwo atsikira mommo.


nimutenge munthu yense mbale yake yofukizamo, nimuike chofukiza m'mwemo, nimubwere nazo, yense mbale yake yofukizamo pamaso pa Yehova, mbale zofukizamo mazana awiri ndi makumi asanu; ndi iwe, ndi Aroni, yense mbale yake yofukizamo.


Koma Yehova akalenga chinthu chatsopano, ndi nthaka ikayasama pakamwa pake, nikawameza ndi zonse ali nazo, nakatsikira iwo kumanda ali ndi moyo; pamenepo mudzadziwa kuti anthu awa anyoza Mulungu.


Ndipo kunali, pakutha iye kunena mau awa onse, nthaka inang'ambika pansi pao;


Chomwecho iwowa, ndi onse anali nao, anatsikira kumanda ali ndi moyo, ndi dziko linasunama pa iwo, ndipo anaonongeka pakati pa msonkhano.


Koma akufa nao mliri ndiwo zikwi khumi ndi zinai mphambu mazana asanu ndi awiri, osawerenga aja adafera chija cha Kora.


ndipo dziko linayasama pakamwa pake, ndi kuwameza pamodzi ndi Kora, pakufa msonkhano uja; muja moto unaononga amuna mazana awiri ndi makumi asanu, nakhala iwo chizindikiro.


Koma sanafe ana aamuna a Kora.


Atate wathu adamwalira m'chipululu, ndipo sanakhale iye pakati pa msonkhano wa iwo akusonkhana kutsutsana ndi Yehova, mu msonkhano wa Kora; koma anafera zoipa zakezake; ndipo analibe ana aamuna.


Musamasadza fuko la mabanja a Akohati kuwachotsa pakati pa Alevi;


ndi chimene anachitira Datani ndi Abiramu, ana a Eliyabu, mwana wa Rubeni; muja nthaka inatsegula pakamwa pake, ndi kuwameza iwo, ndi mabanja ao, ndi mahema ao, ndi za moyo zonse zakuwatsata pakati pa Israele wonse.


Ndipo dziko linathandiza mkaziyo, ndi dziko linatsegula m'kamwa mwake, nilinameza madzi a mtsinje amene chinjoka chinalavula m'kamwa mwake.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa