Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Numeri 4:18 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

18 “Onetsetsani kuti mabanja a fuko la Kohati asachotsedwe kwa Alevi.

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

18 Musamasadza fuko la mabanja a Akohati kuwachotsa pakati pa Alevi;

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

18 Musamasadza fuko la mabanja a Kohati kuwachotsa pakati pa Alevi;

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

18 “Musalole kuti a m'banja la Kohati aonongeke pakati pa Alevi.

Onani mutuwo Koperani




Numeri 4:18
13 Mawu Ofanana  

ndipo Yehova anati kwa iye, “Tsika ukawachenjeze anthu kuti asayesere kudutsa malire kuti adzandione chifukwa ambiri a iwo adzafa.


Wina aliyense amene adzapanga mafuta wonunkhira wofanana nawo kapena kudzozera mafutawa munthu wamba osati wansembe ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.”


Aliyense amene adzapanga wofanana naye kuti asangalale ndi fungo lake ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.”


“Akazi pamodzi ndi ana anu adzaperekedwa kwa Ababuloni. Inuyo simudzapulumuka mʼmanja mwawo koma mfumu ya ku Babuloni idzakugwirani; mzinda uno adzawutentha.”


ndipo dziko linatsekula pakamwa pake ndi kuwameza pamodzi ndi nyumba zawo ndi anthu onse a Kora ndi katundu wawo yense.


Yehova anawuza Mose kuti, “Bwezera ndodo ya Aaroni patsogolo pa Bokosi la Umboni, kuti chikhale chizindikiro cha kuwukira kwawo. Zimenezi zidzathetsa kudandaula kwawo kotsutsana nane, kuopa kuti angafe.”


“Inuyo muzisamalira malo wopatulika ndi guwa lansembe, kuti ukali wa Yehova usawagwerenso Aisraeli.


Kwa Kohati kunali mabanja a Amramu, Aizihara, Ahebroni ndi Auzieli. Awa ndiye anali mabanja a Akohati.


Yehova anawuzanso Mose ndi Aaroni kuti,


Koma muziwachitira izi kuti asafe, akhalebe ndi moyo pamene ayandikira zinthu za ku malo wopatulika kwambiri: Aaroni ndi ana ake aamuna azipita ku malo wopatulika ndi kumamupatsa munthu aliyense ntchito yake ndi zimene ayenera kunyamula.


Yehova anakantha amuna a ku Beti-Semesi 70 chifukwa anasuzumira mʼBokosi la Chipangano cha Yehova. Ndipo anzawo analira chifukwa Yehova anawalanga kwambiri.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa