Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Numeri 12:3 - Buku Lopatulika

Koma munthuyu Mose ndiye wofatsa woposa anthu onse a padziko lapansi.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Koma munthuyu Mose ndiye wofatsa woposa anthu onse a pa dziko lapansi.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Koma Mose anali munthu wofatsa kupambana anthu onse a pa dziko lapansi.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

(Koma Mose anali munthu wodzichepetsa kwambiri kuposa munthu aliyense pa dziko lapansi).

Onani mutuwo



Numeri 12:3
16 Mawu Ofanana  

Yehova agwiriziza ofatsa; atsitsira oipa pansi.


Popeza Yehova akondwera nao anthu ake; adzakometsa ofatsa ndi chipulumutso.


Ndipo Yehova anati kwa Mose, ndi Aroni, ndi Miriyamu modzidzimutsa, Tulukani inu atatu kudza ku chihema chokomanako. Pamenepo anatuluka atatuwo.


Senzani goli langa, ndipo phunzirani kwa Ine; chifukwa ndili wofatsa ndi wodzichepetsa mtima: ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu.


Tauzani mwana wamkazi wa Ziyoni, Taona, mfumu yako idza kwa iwe, wofatsa ndi wokwera pabulu, ndi pa kabulu, mwana wa nyama yonyamula katundu.


Odala ali akufatsa; chifukwa adzalandira dziko lapansi.


Koma ine ndekha Paulo, ndidandaulira inu mwa kufatsa ndi ulere wa Khristu, ine amene pamaso panu ndikhala wodzichepetsa pakati pa inu, koma pokhala kwina ine ndilimbika mtima kwa inu;


Pakuti ndiyesa kuti sindinaperewere konse ndi atumwi oposatu.


Ndakhala wopanda nzeru, mwandichititsa kutero; pakuti inu munayenera kundivomereza; pakuti sindiperewere ndi atumwi oposatu m'kanthu konse, ndingakhale ndili chabe.


Komatu tinakhala ofatsa pakati pa inu, monga m'mene mlezi afukata ana ake a iye yekha;


Ndani ali wanzeru, ndi waluso mwa inu? Aonetsere ndi mayendedwe ake abwino ntchito zake mu nzeru yofatsa.


koma kukhale munthu wobisika wamtima, m'chovala chosaola cha mzimu wofatsa ndi wachete, ndiwo wa mtengo wake wapatali pamaso pa Mulungu.