Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Numeri 12:3 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

3 (Koma Mose anali munthu wodzichepetsa kwambiri kuposa munthu aliyense pa dziko lapansi).

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

3 Koma munthuyu Mose ndiye wofatsa woposa anthu onse a padziko lapansi.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

3 Koma munthuyu Mose ndiye wofatsa woposa anthu onse a pa dziko lapansi.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

3 Koma Mose anali munthu wofatsa kupambana anthu onse a pa dziko lapansi.

Onani mutuwo Koperani




Numeri 12:3
16 Mawu Ofanana  

Yehova amagwiriziza anthu odzichepetsa, koma amagwetsa pansi anthu oyipa.


Pakuti Yehova amakondwera ndi anthu ake; Iye amaveka chipulumutso odzichepetsa.


Nthawi yomweyo Yehova anati kwa Mose, Aaroni ndi Miriamu, “Bwerani ku tenti ya msonkhano nonse atatu.” Ndipo atatuwo anapitadi kumeneko.


Senzani goli langa ndipo phunzirani kwa Ine, pakuti ndine wofatsa ndi wodzichepetsa. Ndipo inu mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu.


“Uza mwana wamkazi wa Ziyoni, taona, mfumu yako ikubwera kwa iwe, yofatsa ndi yokwera pa bulu, pa kamwana ka bulu, mwana wa nyama yonyamula katundu.”


Odala ndi amene ali ofatsa, chifukwa adzalandira dziko lapansi.


Mwa kufatsa ndi kuleza mtima kwa Khristu, ndikukupemphani, ine Paulo amene anthu ena amati ndimachita manyazi tikaonana maso ndi maso ndi inu, koma wosaopa pamene ndili kutali nanu!


Komatu sindikuganiza kuti ndine wotsika kwambiri kwa “atumwi apamwamba.”


Ndadzisandutsa wopusa, koma inu mwandichititsa zimenezi. Ndinu amene munayenera kundichitira umboni. Ngakhale kuti sindine kanthu, koma sindine wochepetsetsa kwa “atumwi apamwamba” aja.


Ngati atumwi a Khristu tikanatha kukhala cholemetsa kwa inu, mʼmalo mwake tinali ngati ana aangʼono pakati panu. Monga mmene amayi amasamalira ana awo angʼono,


Ndani mwa inu amene ndi wanzeru ndi womvetsa zinthu? Mulekeni aonetse ndi makhalidwe ake abwino kuti nzeru ndiye zikutsogolera kudzichepetsa kwake ndi zochita zake


Mʼmalo mwake kudzikongoletsa kwanu kukhale kwa munthu wa mʼkatimo, kukongola kosatha kwa mtima ofatsa ndi mzimu wachete, zimene ndi za mtengowapatali pamaso pa Mulungu.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa