Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Numeri 10:35 - Buku Lopatulika

Ndipo kunali pakuchokera kunka nalo likasa, Mose anati, Ukani Yehova, abalalike adani anu; akuda Inu athawe pamaso panu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo kunali pakuchokera kunka nalo likasa, Mose anati, Ukani Yehova, abalalike adani anu; akuda Inu athawe pamaso panu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Nthaŵi iliyonse pamene Bokosi lachipangano linkanyamuka, Mose ankati, “Dzambatukani, Inu Chauta, muŵamwaze adani anu. Onse odana nanu athaŵe akakuwonani.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nthawi iliyonse imene Bokosi la Chipangano likunyamuka, Mose ankanena kuti, “Dzukani, Inu Yehova! Adani anu abalalike; Odana nanu athawe pamaso panu.

Onani mutuwo



Numeri 10:35
10 Mawu Ofanana  

Ukani, Yehova, lowani ku mpumulo wanu; Inu ndi hema wa mphamvu yanu.


Chipulumutso ncha Yehova; dalitso lanu likhale pa anthu anu.


Ukani, Yehova, asalimbike munthu; amitundu aweruzidwe pankhope panu.


Adzandiukira ndani kutsutsana nao ochita zoipa? Adzandilimbikira ndani kutsutsana nao ochita zopanda pake?


Galamuka, galamuka, khala ndi mphamvu, mkono wa Yehova; galamuka monga masiku akale, mibadwo ya nthawi zakale. Kodi si ndiwe amene unadula Rahabu zipinjirizipinjiri; amene unapyoza chinjoka chamnyanja chija?


ndikanola lupanga langa lonyezimira, ndi dzanja langa likagwira chiweruzo; ndidzabwezera chilango ondiukira, ndi kulanga ondida.


Ndipo awabwezera onse akudana ndi Iye, pamaso pao, kuwaononga; sachedwa naye wakudana ndi Iye, ambwezera pamaso pake.


Ndipo pamene anthu anafika ku zithandozo, akulu a Israele anati, Yehova anatikanthiranji lero pamaso pa Afilisti? Tikadzitengere likasa la chipangano la Yehova ku Silo, kuti likabwera pakati pa ife, lidzatipulumutsa m'dzanja la adani athu.