Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Mateyu 8:1 - Buku Lopatulika

Ndipo pakutsika pake paphiripo, inamtsata mipingo yambiri ya anthu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo pakutsika pake paphiripo, inamtsata mipingo yambiri ya anthu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Yesu atatsika kuphiri kuja, anthu ambirimbiri adamtsatira.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Iye atatsika ku phiri kuja, anthu ambirimbiri anamutsata.

Onani mutuwo



Mateyu 8:1
12 Mawu Ofanana  

Koma Yesu m'mene anadziwa, anachokera kumeneko: ndipo anamtsata Iye anthu ambiri; ndipo Iye anawachiritsa iwo onse,


Ndipo makamu ambiri a anthu anadza kwa Iye, ali nao opunduka miyendo, akhungu, osalankhula, opunduka ziwalo, ndi ena ambiri, nawakhazika pansi pa mapazi ake: ndipo Iye anawachiritsa;


Ndipo makamu aakulu a anthu anamtsata; ndipo Iye anawachiritsa kumeneko.


Ndipo pamene iwo analikutuluka mu Yeriko, khamu lalikulu la anthu linamtsata Iye.


Ndipo inamtsata mipingomipingo ya anthu ochokera ku Galileya, ndi ku Dekapoli ndi ku Yerusalemu, ndi ku Yudeya, ndi ku tsidya lija la Yordani.


pakuti anawaphunzitsa monga mwini mphamvu, wosanga alembi ao.


Ndipo Yesu, poona makamu ambiri a anthu akumzungulira Iye, analamulira ophunzira amuke kutsidya lina.


Ndipo onani, wakhate anadza namgwadira Iye, nanena, Ambuye ngati mufuna mungathe kundikonza.


Ndipo Yesu anachokako pamodzi ndi ophunzira ake nanka kunyanja: ndipo linamtsata khamu lalikulu la a ku Galileya, ndi a ku Yudeya,


Koma makamaka mbiri yake ya Iye inabuka: ndipo mipingo yambiri ya anthu inasonkhana kudzamvera, ndi kudzachiritsidwa nthenda zao.