Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 73:2 - Buku Lopatulika

Koma ine, ndikadagwa; mapazi anga akadaterereka.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Koma ine, ndikadagwa; mapazi anga akadaterereka.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Koma ine ndinali pafupi kuphunthwa, mapazi anga anali pafupi kuterereka.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Koma kunena za ine, mapazi anga anali pafupi kuterereka; ndinatsala pangʼono kugwa.

Onani mutuwo



Masalimo 73:2
15 Mawu Ofanana  

Ndipo Davide anati kwa Solomoni mwana wake, Kunena za ine, kumtima kwanga kudati, ndilimangire dzina la Yehova Mulungu wanga nyumba.


Munthu wosatekeseka apeputsa tsoka mumtima mwake, limlindira woterereka mapazi ake.


Kodi ine, kudandaula kwanga, ndidandaulira munthu? Ndipo ndilekerenji kupsa mtima?


Pakuti munalanditsa moyo wanga kuimfa, maso anga kumisozi, mapazi anga, ndingagwe.


Koma ine ndidzapenyerera nkhope yanu m'chilungamo, ndidzakhuta mtima ndi maonekedwe anu, pamene ndidzauka.


M'mayendedwe anga ndasunga mabande anu, mapazi anga sanaterereke.


Koma ine, pakudwala iwowa, chovala changa ndi chiguduli. Ndinazunza moyo wanga ndi kusala; ndipo pemphero langa linabwera kuchifuwa changa.


Pakuti ndinati, Asakondwerere ine; pakuterereka phazi langa, asadzikuze pa ine.


Koma ine, mwa kuchuluka kwa chifundo chanu ndidzalowa m'nyumba yanu; ndidzagwada kuyang'ana Kachisi wanu woyera ndi kuopa Inu.


Pamene ndinati, Literereka phazi langa, chifundo chanu, Yehova, chinandichirikiza.


Ndikadakhala m'zoipa zonse, m'kati mwa msonkhano ndi khamu la anthu.


Ndipo ngati kutumikira Yehova kukuipirani mudzisankhire lero amene mudzamtumikira, kapena milungu imene anaitumikira makolo anu okhala tsidya lija la mtsinje, kapena milungu ya Aamori amene mukhala m'dziko lao; koma ine, ndi a m'nyumba yanga, tidzatumikira Yehova.


Ndipo inenso, kukhale kutali ndi ine, kuchimwira Yehova ndi kuleka kukupemphererani; koma ndidzakulangizani njira yabwino ndi yolungama.


Adzasunga mapazi a okondedwa ake, koma oipawo adzawakhalitsa chete mumdima; pakuti palibe munthu adzapambana ndi mphamvu.