Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




1 Samueli 2:9 - Buku Lopatulika

9 Adzasunga mapazi a okondedwa ake, koma oipawo adzawakhalitsa chete mumdima; pakuti palibe munthu adzapambana ndi mphamvu.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

9 Adzasunga mapazi a okondedwa ake, koma oipawo adzawakhalitsa chete mumdima; pakuti palibe munthu adzapambana ndi mphamvu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

9 “Anthu okhulupirika Iye adzatchinjiriza moyo wao, koma anthu oipa adzazimirira mu mdima, pakuti munthu sapambana ndi mphamvu zake.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

9 Iye adzateteza moyo wa anthu okhulupirika koma anthu oyipa adzawonongedwa mu mdima. “Pakuti munthu sapambana ndi mphamvu zake.

Onani mutuwo Koperani




1 Samueli 2:9
41 Mawu Ofanana  

Adzamkankha achoke kukuunika alowe kumdima; adzampirikitsa achoke m'dziko lokhalamo anthu.


Uwakwirire pamodzi m'fumbi, uzimange nkhope zao pobisika.


Potero aumphawi ali nacho chiyembekezo, ndi mphulupulu yatsekedwa pakamwa.


Ndipo udzapeza kuti pahema pako mpa mtendere; nudzazonda za m'banja mwako osasowapo kanthu.


Pakuti Yehova adziwa mayendedwe a olungama; koma mayendedwe a oipa adzatayika.


Ndipo anawatulutsa pamodzi ndi siliva ndi golide: ndi mwa mafuko ao munalibe mmodzi wokhumudwa.


Sadzalola phazi lako literereke: Iye amene akusunga sadzaodzera.


Yehova ndiye wakukusunga; Yehova ndiye mthunzi wako wa kudzanja lako lamanja.


Yehova adzasungira kutuluka kwako ndi kulowa kwako, kuyambira tsopano kufikira nthawi zonse.


Yehova asunga onse akukondana naye; koma oipa onse adzawaononga.


Yehova, musandichititse manyazi; pakuti ndafuulira kwa Inu, oipa achite manyazi, atonthole m'manda.


Pakuti Yehova akonda chiweruzo, ndipo sataya okondedwa ake. Asungika kosatha, koma adzadula mbumba za oipa.


Pamene ndinati, Literereka phazi langa, chifundo chanu, Yehova, chinandichirikiza.


Inu okonda Yehova, danani nacho choipa: Iye asunga moyo wa okondedwa ake; awalanditsa m'manja mwa oipa.


Mtima wa munthu ulingalira njira yake; koma Yehova ayendetsa mapazi ake.


kuti atchinjirize njira za chiweruzo, nadikire khwalala la opatulidwa ake.


pakuti Yehova adzalimbitsa mtima wako, nadzasunga phazi lako lingakodwe.


Inde masiku ake onse amadya mumdima, ndipo zimchulukira chisoni ndi nthenda ndi mkwiyo.


Ndinabweranso ndi kuzindikira pansi pano kuti omwe athamanga msanga sapambana m'liwiro, ngakhale olimba sapambana m'nkhondo, ngakhale anzeru sapeza zakudya, ngakhale ozindikira bwino salemera, ngakhale odziwitsa sawakomera mtima; koma yense angoona zomgwera m'nthawi mwake.


Ine Yehova ndiusunga uwo; ndidzauthirira madzi nthawi zonse; ndidzausunga usiku ndi usana, kuti angauipse.


Khala iwe chete, lowa mumdima, mwana wamkazi wa Ababiloni; pakuti sudzatchedwanso mkazi wa maufumu.


Tikhaliranji ife? Tasonkhanani, tilowe m'mizinda yamalinga, tikhale chete m'menemo; pakuti Yehova Mulungu wathu watikhalitsa ife chete, natipatsa ife madzi a ndulu timwe, pakuti tamchimwira Yehova.


Atero Yehova, wanzeru asadzitamandire m'nzeru zake, wamphamvu asadzitamandire m'mphamvu yake, wachuma asadzitamandire m'chuma chake;


Koma ndi chigumula chosefukira adzatha konse malo ake, nadzapirikitsira adani ake kumdima.


Tsikulo ndi tsiku la mkwiyo, tsiku la msauko ndi lopsinja tsiku la bwinja, ndi chipasuko, tsiku la mdima ndi la chisisira, tsiku la mitambo ndi lakuda bii;


Pamenepo anayankha, nanena kwa ine, ndi kuti, Awa ndi mau a Yehova kwa Zerubabele, Ndi khamu la nkhondo ai, ndi mphamvu ai, koma ndi Mzimu wanga, ati Yehova wa makamu.


Yehova akudalitse iwe, nakusunge;


koma anawo a Ufumu adzatayidwa kumdima wakunja; komweko kudzakhala kulira ndi kukukuta mano.


Ndipo tidziwa kuti zinthu zilizonse chizinena chilamulo chizilankhulira iwo ali nacho chilamulo; kuti pakamwa ponse patsekedwe, ndi dziko lonse lapansi litsutsidwe ndi Mulungu;


Inde akonda mitundu ya anthu; opatulidwa ake onse ali m'dzanja mwanu; ndipo akhala pansi ku mapazi anu; yense adzalandirako mau anu.


amene musungidwa ndi mphamvu ya Mulungu mwa chikhulupiriro, kufikira chipulumutso chokonzeka kukavumbulutsidwa nthawi yotsiriza.


Aphunzitsi onamawo ndiwo akasupe opanda madzi, nkhungu yokankhika ndi mkuntho; amene mdima wakuda bii uwasungikira.


Yuda, kapolo wa Yesu Khristu, ndi mbale wa Yakobo, kwa iwo oitanidwa, okondedwa mwa Mulungu Atate, ndi osungidwa ndi Yesu Khristu:


mafunde oopsa a nyanja, akuwinduka thovu la manyazi a iwo okha; nyenyezi zosokera, zimene mdima wakuda bii udazisungikira kosatha.


Okondedwa, pakuchita changu chonse chakukulemberani za chipulumutso cha ife tonse, ndafulumidwa mtima ine kukulemberani ndi kudandaulira kuti mulimbanetu chifukwa cha chikhulupiriro chapatsidwa kamodzi kwa oyera mtima.


Chifukwa chake tsono, mbuye wanga, pali Yehova, ndipo pali moyo wanu, popeza Yehova anakuletsani kuti mungakhetse mwazi, ndi kudzibwezera chilango ndi dzanja la inu nokha, chifukwa chake adani anu, ndi iwo akufuna kuchitira mbuye wanga choipa, akhale ngati Nabala.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa