Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 26:12 - Buku Lopatulika

Phazi langa liponda pachidikha, m'misonkhano ndidzalemekeza Yehova.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Phazi langa liponda pachidikha, m'masonkhano ndidzalemekeza Yehova.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ndili wokhazikika pa malo opanda zovuta, ndipo ndidzatamanda Chauta pa msonkhano waukulu.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndayima pa malo wopanda zovuta ndipo ndidzatamanda Yehova mu msonkhano waukulu.

Onani mutuwo



Masalimo 26:12
11 Mawu Ofanana  

Amkwezenso mu msonkhano wa anthu, namlemekeze pokhala akulu.


Aleluya. Ndidzayamika Yehova ndi mtima wonse, mu upo wa oongoka mtima, ndi mumsonkhano.


Kumene akwerako mafuko, ndiwo mafuko a Yehova; akhale mboni ya kwa Israele, Ayamike dzina la Yehova.


kuti ndimveketse mau a chiyamiko, ndi kulalikira ntchito zanu zonse zozizwa.


Mundiphunzitse njira yanu, Yehova, munditsogolere panjira yachidikha, chifukwa cha adani anga.


Ndipo anandikweza kunditulutsa m'dzenje la chitayiko, ndi m'thope la pachithaphwi; nandipondetsa pathanthwe, nakhazika mayendedwe anga.


Apo pali Benjamini wamng'ono, wakuwachita ufumu, akulu a Yuda, ndi a upo wao, akulu a Zebuloni, akulu a Nafutali.


Woyenda moongoka amayenda osatekeseka; koma wokhotetsa njira zake adzadziwika.


Ndi kuti, Ndidzalalikira dzina lanu kwa abale anga, pakati pa Mpingo ndidzakuimbirani.


Adzasunga mapazi a okondedwa ake, koma oipawo adzawakhalitsa chete mumdima; pakuti palibe munthu adzapambana ndi mphamvu.