Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 112:2 - Buku Lopatulika

Mbeu yake idzakhala yamphamvu padziko lapansi; mbadwo wa oongoka mtima udzadalitsidwa.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Mbeu yake idzakhala yamphamvu pa dziko lapansi; mbadwo wa oongoka mtima udzadalitsidwa.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Zidzukulu zake zidzakhala zamphamvu pa dziko lapansi. Ana a munthuyo adzakhala odala.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko; mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.

Onani mutuwo



Masalimo 112:2
12 Mawu Ofanana  

Ndipo ndidzalimbitsa pangano langa ndi Ine ndi iwe pa mbeu zako za pambuyo pako m'mibadwo yao, kuti likhale pangano la nthawi zonse, kuti ndikhale Mulungu wako ndi wa mbeu zako za pambuyo pako.


Ndipo panali atafa Abrahamu, Mulungu anamdalitsa Isaki mwana wake; ndipo Isaki anakhala pa Beere-Lahai-Roi.


Ana a atumiki anu adzakhalitsa, ndi mbeu zao zidzakhazikika pamaso panu.


Moyo wake udzakhala mokoma; ndi mbumba zake zidzalandira dziko lapansi.


Tsiku lonse achitira chifundo, nakongoletsa; ndipo mbumba zake zidalitsidwa.


Zoonadi, wochimwa sadzapulumuka chilango; koma mbeu ya olungama idzalanditsidwa.


Wabwino asiyira zidzukulu zake cholowa chabwino; koma wochimwa angosungira wolungama chuma chake.


Wolungama woyenda mwangwiro, anake adala pambuyo pake.


ndipo ndidzawapatsa mtima umodzi ndi njira imodzi, kuti andiope Ine masiku onse; kuwachitira zabwino, ndi ana ao pambuyo pao;


chipande chimodzi chagolide cha masekeli khumi, chodzala ndi chofukiza;


Pakuti lonjezano lili kwa inu, ndi kwa ana anu, ndi kwa onse akutali, onse amene Ambuye Mulungu wathu adzaitana.