Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 102:5 - Buku Lopatulika

Chifukwa cha liu la kubuula kwanga mnofu wanga umamatika kumafupa anga.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Chifukwa cha liu la kubuula kwanga mnofu wanga umamatika kumafupa anga.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ndaonderatu ngati munthu wachitopa, ntchito yanga ndi kubuula nthaŵi zonse.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chifukwa cha kubuwula kwanga kofuwula ndatsala chikopa ndi mafupa okhaokha.

Onani mutuwo



Masalimo 102:5
10 Mawu Ofanana  

Atuluka ngati duwa, nafota; athawa ngati mthunzi, osakhalitsa.


Fupa langa laumirira pa khungu langa ndi mnofu wanga, ndipo ndapulumuka ndili nazo nkhama za mano anga.


Ndalema nako kuusa moyo kwanga; ndiyandamitsa kama wanga usiku wonse; mphasa yanga ndiolobza ndi misozi yanga.


Chokani kwa ine, nonsenu akuchita zopanda pake; pakuti wamva Yehova mau a kulira kwanga.


Mamawa uphuka bwino; madzulo ausenga, nuuma.


Mtima wosekerera uchiritsa bwino; koma mzimu wosweka uphwetsa mafupa.


Maonekedwe ao ada koposa makala, sazindikirika m'makwalala; khungu lao limamatira pa mafupa ao, lakhwinyata, lasanduka ngati ndodo.


Ndipo popeza munthuyo adatero chaka ndi chaka, popita mkaziyo kunyumba ya Yehova, mnzakeyo amamputa; chifukwa chake iye analira misozi, nakana kudya.