Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 102:3 - Buku Lopatulika

Popeza masiku anga akanganuka ngati utsi, ndi mafupa anga anyeka ngati nkhuni.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Popeza masiku anga akanganuka ngati utsi, ndi mafupa anga anyeka ngati nkhuni.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Masiku anga amangopita ngati utsi, ndipo thupi langa likuyaka ngati ng'anjo.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Pakuti masiku anga akupita ngati utsi; mafupa anga akunyeka ngati nkhuni zoyaka.

Onani mutuwo



Masalimo 102:3
11 Mawu Ofanana  

Khungu langa lada, nilindifundukira; ndi mafupa anga awawa ndi kutentha kwao.


Popeza ndakhala ngati thumba lofukirira; koma sindiiwala malemba anu.


Musandibisire ine nkhope yanu; musachotse kapolo wanu ndi kukwiya. Inu munakhala thandizo langa; musanditaye, ndipo musandisiye Mulungu wa chipulumutso changa.


Pakuti moyo wanga watha ndi chisoni, ndi zaka zanga zatha ndi kuusa moyo. Mphamvu yanga yafooka chifukwa cha kusakaza kwanga, ndi mafupa anga apuwala.


Pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa; ndipo chifukwa cha dzina lanu ndiyendetseni bwino, ndipo nditsogolereni.


Pakuti oipa adzatayika, ndipo adani ake a Yehova adzanga mafuta a anaankhosa; adzanyeka, monga utsi adzakanganuka.


Mumnofu mwanga mulibe chamoyo chifukwa cha ukali wanu; ndipo m'mafupa anga simuzizira, chifukwa cha cholakwa changa.


Anatumiza moto wochokera kumwamba kulowa m'mafupa anga, unawagonjetsa; watchera mapazi anga ukonde, wandibwezera m'mbuyo; wandipululutsa ndi kundilefula tsiku lonse.


Wagugitsa thupi langa ndi khungu langa, nathyola mafupa anga.


inu amene simudziwa chimene chidzagwa mawa. Moyo wanu uli wotani? Pakuti muli utsi, wakuonekera kanthawi, ndi pamenepo ukanganuka.