Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Genesis 13:12 - Buku Lopatulika

Ndipo Abramu anakhala m'dziko la Kanani, ndipo Loti anakhala m'mizinda ya m'chigwa, nasendeza hema wake kufikira ku Sodomu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Abramu anakhala m'dziko la Kanani, ndipo Loti anakhala m'midzi ya m'chigwa, nasendeza hema wake kufikira ku Sodomu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Abramu adakhala m'dziko la Kanani, koma Loti adakhazikika pakati pa mizinda yam'chigwa, nakamanga hema pafupi ndi mzinda wa Sodomu.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Abramu anakhala mʼdziko la Kanaani, pamene Loti anakakhala pakati pa mizinda ikuluikulu ya mʼchigwamo. Anamanga tenti yake pafupi ndi Sodomu.

Onani mutuwo



Genesis 13:12
10 Mawu Ofanana  

Ndipo Loti anasankha chigwa chonse cha Yordani; ndipo Loti anachoka ulendo wake kunka kum'mawa: ndipo analekana wina ndi mnzake.


Ndipo anagwira Loti mwana wa Abramu amene anakhala mu Sodomu, ndi chuma chake, namuka.


iwo anathira nkhondo pa Bera mfumu ya Sodomu, ndi pa Birisa, mfumu ya Gomora, ndi pa Sinabe mfumu ya Adima, ndi pa Semebera mfumu ya Zeboimu, ndi pa mfumu ya Bela (kumeneko ndi ku Zowari).


Ndipo anadza ku Sodomu madzulo amithenga awiri; ndipo Loti anakhala pa chipata cha Sodomu, ndipo Loti anaona iwo, nauka kuti akakomane nao, ndipo anaweramitsa pansi nkhope yake.


Ndipo Yehova anavumbitsa pa Sodomu ndi pa Gomora miyala ya sulufure ndi moto kutuluka kwa Mulungu kumwamba;


ndipo anaononga mizindayo, ndi chigwa chonse, ndi onse akukhala m'mizindamo, ndi zimene zimera panthaka.


Ndipo panali pamene Mulungu anaononga mizinda ya m'chigwa, Mulungu anakumbukira Abrahamu, natulutsa Loti pakati pa chionongeko, pamene anaononga mizinda m'mene anakhalamo Loti.


Ndidana nao msonkhano wa ochimwa, ndipo sindidzakhala nao pansi ochita zoipa.


Musanyengedwe; mayanjano oipa aipsa makhalidwe okoma.