Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 40:16 - Buku Lopatulika

Anatero Mose; monga mwa zonse Yehova adamuuza, momwemo anachita.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Anatero Mose; monga mwa zonse Yehova adamuuza, momwemo anachita.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Mose adachita zonse, monga momwe Chauta adamlamulira.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mose anachita zonse monga Yehova anamulamulira.

Onani mutuwo



Eksodo 40:16
19 Mawu Ofanana  

Chotero anachita Nowa, monga mwa zonse anamlamulira iye Mulungu, momwemo anachita.


nuwadzoze, monga unadzoza atate wao, kuti andichitire ntchito ya nsembe; ndi kudzozedwa kwao kuwakhalire unsembe wosatha mwa mibadwo yao.


Ndipo Mose ndi Aroni anachita monga Yehova anawalamulira, momwemo anachita.


Kuchilamulo ndi kuumboni! Ngati iwo sanena malinga ndi mau awa, ndithu sadzaona mbandakucha.


Ndipo ndinapita, ndinaubisa pa Yufurate, monga Yehova anandiuza ine.


Ndipo Mose anatenga ana a Aroni, nawaveka malaya a m'kati, nawamanga m'chuuno ndi mipango, nawamanga akapa; monga Yehova adzauza Mose.


Koma anatsuka matumbo ndi miyendo ndi madzi; ndi Mose anatentha mphongo yonse paguwa la nsembe; ndiyo nsembe yopsereza yochita fungo lokoma; ndiyo nsembe yamoto ya kwa Yehova; monga Yehova adamuuza Mose.


Naika nduwirayo pamutu pake; ndi panduwira, pamphumi pake anaika golide waphanthiphanthi, ndiwo korona wopatulika; monga Yehova adauza Mose.


Monga Yehova analamula Mose, momwemo anawawerenga m'chipululu cha Sinai.


Ngakhale masiku awiri, kapena mwezi, kapena masiku ambiri, pokhalitsa mtambo pamwamba pa chihema ndi kukhalapo, ana a Israele anakhala m'chigono, osayenda ulendo; koma pakukwera uwu, anayenda ulendo.


ndi kuwaphunzitsa, asunge zinthu zonse zimene ndinakulamulani inu; ndipo onani, Ine ndili pamodzi ndi inu masiku onse, kufikira chimaliziro cha nthawi ya pansi pano.


Komatu pano pafunika za adindo, kuti munthu akhale wokhulupirika.


Chilichonse ndikuuzani, muchisamalire kuchichita; musamaonjezako, kapena kuchepsako.


Ndipo tsopano, Israele, tamverani malemba ndi maweruzo, amene ndikuphunzitsani muwachite; kuti mukhale ndi moyo, ndi kulowa, ndi kulandira dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu akupatsani.


amene anakhala wokhulupirika kwa Iye adamuikayo, monganso Mose m'nyumba yake yonse.


Ndipo Mosetu anali wokhulupirika m'nyumba yake yonse, monga mnyamata, achitire umboni izi zidzalankhulidwazi;