Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 17:15 - Buku Lopatulika

Ndipo Mose anamanga guwa la nsembe, nalitcha dzina lake Yehova Nisi:

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Mose anamanga guwa la nsembe, nalitcha dzina lake Yehova Nisi:

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ndipo Mose adamanga guwa nalitcha kuti, “Chauta ndiye mbendera yanga.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mose anamanga guwa lansembe ndipo analitcha Yehova Chipambano Changa (Yehova Nisi).

Onani mutuwo



Eksodo 17:15
9 Mawu Ofanana  

Ndipo Yehova anaonekera kwa Abramu nati, Ndidzapatsa mbeu yako dziko lino: pamenepo anammangira Yehova guwa la nsembe amene anamuonekera iye.


Ndipo iye anachoka kumeneko kunka kuphiri la kum'mawa kwa Betele, namanga hema wake; Betele anali kumadzulo, ndi Ai anali kum'mawa: kumeneko ndipo anammangira Yehova guwa la nsembe, naitanira dzina la Yehova.


Ndipo Abrahamu anatcha dzina lake la malowo Yehova-Yire: monga ati lero lomwe, M'phiri la Yehova chidzaoneka.


Ndipo anamanga pamenepo guwa la nsembe, natcha pamenepo El-Elohe-Israele.


Koma mwapatsa mbendera akuopa Inu, aikweze chifukwa cha choonadi.


Ndipo Mose analembera mau onse a Yehova, nalawira kuuka mamawa, namanga guwa la nsembe patsinde paphiri, ndi zoimiritsa khumi ndi ziwiri, kwa mafuko khumi ndi awiri a Israele.


Ndipo upange guwa la nsembe la mtengo wakasiya, utali wake mikono isanu, ndi kupingasa kwake mikono isanu, guwa la nsembelo likhale laphwamphwa, ndi msinkhu wake mikono itatu.


Pakuchiona Aroni, anamanga guwa la nsembe patsogolo pake; ndipo Aroni anafuula nati, Mawa aliko madyerero a Yehova.


Pamenepo Gideoni anammangira Yehova guwa la nsembe pomwepo; nalitcha Yehova-ndiye-mtendere; likali mu Ofura wa Aabiyezere ndi pano pomwe.