Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Samueli 5:9 - Buku Lopatulika

Ndipo Davide anakhala m'linga muja, nalitcha mzinda wa Davide. Davide namanga linga pozinga ponse kuyambira ku Milo ndi m'kati momwe.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Davide anakhala m'linga muja, nalitcha mudzi wa Davide. Davide namanga linga pozinga ponse kuyambira ku Milo ndi m'kati momwe.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Tsono Davide adakhala mu mzinda wamalinga uja nautchula dzina lakuti, “Mzinda wa Davide.” Ndipo adamanga mzinda kuzungulira deralo kuyambira ku malo komwe kale kunali chidikha, kuvuma kwa phiri mpaka m'kati mwake.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Tsono Davide anakhazikika mu lingamo ndipo mzindawu anawutcha, Mzinda wa Davide. Iye anamanga malo onse ozungulira kuyambira ku matsitso ozungulira khoma.

Onani mutuwo



2 Samueli 5:9
16 Mawu Ofanana  

Chinkana anatero Davide anathyola linga la Ziyoni, lomwelo ndilo mzinda wa Davide.


Ndipo tsiku lija Davide anati, Aliyense akakantha Ayebusi, aponye m'madzi opuwala ndi akhungu amene moyo wa Davide udana nao. Chifukwa chake akuti, Akhungu ndi opuwala sangalowe m'nyumbamo.


Momwemo Davide sanafune kudzitengera likasa la Yehova lidze kumzinda wa Davide; koma Davide analipambutsira kunyumba ya Obededomu Mgiti.


Ndipo chifukwa chakukweza iye dzanja lake pa mfumu ndi chimenechi: Solomoni anamanga Milo, namanganso pogumuka pa linga la mzinda wa Davide atate wake.


Ndipo Davide anagona pamodzi ndi makolo ake, naikidwa m'mzinda wa Davide.


Ndipo chifukwa chake cha msonkho uja anausonkhetsa mfumu Solomoni ndi chimenechi; kuti amange nyumba ya Yehova, ndi nyumba ya iye yekha, ndi Milo, ndi linga la Yerusalemu, ndi Hazori, ndi Megido, ndi Gezere.


Koma mwana wamkazi wa Farao anatuluka m'mzinda wa Davide kukwera kunyumba yake adammangira Solomoni, pamenepo iye anamanganso Milo.


Ndipo anyamata ake ananyamuka, napangana, nakantha Yowasi kunyumba ya Milo potsikira ku Sila.


Pakuti Yozakara mwana wa Simeati, ndi Yehozabadi mwana wa Somere, anyamata ake, anamkantha, nafa iye; ndipo anamuika kwa makolo ake m'mzinda wa Davide; ndi Amaziya mwana wake anakhala mfumu m'malo mwake.


Ndipo anamanga mzinda pozungulira pake, kuyambira ku Milo ndi pozungulira pake; ndi Yowabu anakonzanso potsala pa mzinda.


Ndipo analimbika mtima, namangitsa linga lonse mopasuka, nalikweza mpaka pansanja, ndi linga lina kunja kwake, nalimbitsa Milo m'mzinda wa Davide, napanga zida ndi zikopa zochuluka.


Ndi Chipata cha ku Kasupe anachikonza Salumu mwana wa Kolihoze mkulu wa dziko la Mizipa anachimanga, nachikomaniza pamwamba pake, naika zitseko zake, zokowera zake, ndi mipiringidzo yake; ndiponso linga la dziwe la Sela pamunda wa mfumu, ndi kufikira kumakwerero otsikira kumzinda wa Davide.


Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda woundana bwino:


Eya Ariyele, Ariyele, mzinda umene Davide anamangapo zithando! Onjezerani chaka ndi chaka; maphwando afikenso;


koma ngati simunatero, utuluke moto kwa Abimeleki, nunyeketse eni ake a ku Sekemu ndi nyumba ya Milo; nutuluke moto kwa eni ake a ku Sekemu, ndi kunyumba yake ya Milo, nunyeketse Abimeleki.


Pamenepo anasonkhana eni ake onse a ku Sekemu, ndi nyumba yonse ya Milo, namuka namlonga Abimeleki ufumu pa thundu wa choimiritsa chili mu Sekemu.