Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Akorinto 4:1 - Buku Lopatulika

Chifukwa chake popeza tili nao utumiki umene, monga talandira chifundo, sitifooka;

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Chifukwa chake popeza tili nao utumiki umene, monga talandira chifundo, sitifooka;

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Mulungu mwa chifundo chake adatipatsa ntchitoyi, nchifukwa chake sititaya mtima.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Choncho popeza mwachifundo cha Mulungu tili ndi utumiki uwu, sititaya mtima.

Onani mutuwo



2 Akorinto 4:1
19 Mawu Ofanana  

Ngakhale anyamata adzalefuka ndi kulema ndi amisinkhu adzagwa ndithu:


koma iwo amene alindira Yehova adzatenganso mphamvu; adzauluka pamwamba ndi mapiko monga ziombankhanga; adzathamanga koma osalema; adzayenda koma osalefuka.


Munati, Kalanga ine tsopano! Pakuti Yehova waonjezera chisoni pa zowawa zanga; ndalema ndi kubuula kwanga, sindipeza kupuma.


Ndipo anawanenera fanizo lakuti ayenera iwo kupemphera nthawi zonse, osafooka mtima;


Ndipo Apolo nchiyani, ndi Paulo nchiyani? Atumiki amene munakhulupirira mwa iwo, yense monga Ambuye anampatsa.


Koma kunena za anamwali, ndilibe lamulo la Ambuye; koma ndikuuzani choyesa iye, monga wolandira chifundo kwa Ambuye kukhala wokhulupirika.


Pokhala nacho tsono chiyembekezo chotere, tilankhula ndi kukhazikika mtima kwakukulu,


amenenso anatikwaniritsa ife tikhale atumiki a pangano latsopano; si la chilembo, koma la mzimu; pakuti chilembo chipha, koma mzimu uchititsa moyo.


Chifukwa chake sitifooka; koma ungakhale umunthu wathu wakunja uvunda, wa m'kati mwathu ukonzedwa kwatsopano tsiku ndi tsiku.


Koma zinthu zonse zichokera kwa Mulungu amene anatiyanjanitsa kwa Iye yekha mwa Khristu, natipatsa utumiki wa chiyanjanitso;


Koma tisaleme pakuchita zabwino; pakuti pa nyengo yake tidzatuta tikapanda kufooka.


Mwa ichi ndipempha kuti musade mtima m'zisautso zanga chifukwa cha inu, ndiwo ulemerero wanu.


Ndikhoza zonse mwa Iye wondipatsa mphamvuyo.


Koma inu, abale, musaleme pakuchita zabwino.


ndingakhale kale ndinali wamwano, ndi wolondalonda, ndi wachipongwe; komatu anandichitira chifundo, popeza ndinazichita wosazindikira, wosakhulupirira;


Pakuti talingirirani Iye amene adapirira ndi ochimwa otsutsana naye kotere, kuti mungaleme ndi kukomoka m'moyo mwanu.


inu amene kale simunali anthu, koma tsopano muli anthu a Mulungu; amene kale simunalandire chifundo, koma tsopano mwalandira chifundo.


ndipo uli nacho chipiriro, ndipo walola chifukwa cha dzina langa, wosalema.